Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mika 2:7 - Buku Lopatulika

7 Kodi adzati, Nyumba ya Yakobo iwe, Mzimu wa Yehova waperewera kodi? Izi ndi ntchito zake kodi? Mau anga samchitira zokoma kodi, iye amene ayenda choongoka?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Kodi adzati, Nyumba ya Yakobo iwe, Mzimu wa Yehova waperewera kodi? Izi ndi ntchito zake kodi? Mau anga samchitira zokoma kodi, iye amene ayenda choongoka?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Monga zoterezi nzoyenera kuzinena, inu a banja la Yakobe? Kodi kuleza mtima kwa Chauta kwatheratu? Kodi zimenezi nzimene adachita? Kodi mau ake sadzetsa zabwino kwa munthu woyenda molungama?”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?

Onani mutuwo Koperani




Mika 2:7
31 Mawu Ofanana  

Munachitira mtumiki wanu chokoma, Yehova, monga mwa mau anu.


Inu ndinu wabwino, ndi wakuchita zabwino; mundiphunzitse malemba anu.


Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo, nanena zoonadi mumtima mwake.


Pa woyera mtima mukhala woyera mtima; pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.


Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.


Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima; koma akuchita zoipa adzaonongeka.


Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.


Woyenda moongoka mtima aopa Yehova; koma wokhota m'njira yake amnyoza.


Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;


Woyenda mwangwiro adzapulumuka; koma wokhota m'mayendedwe ake adzagwa posachedwa.


Chifukwa chanji ndinafika osapeza munthu? Ndi kuitana koma panalibe wina woyankha? Kodi dzanja langa lafupika konse, kuti silingathe kuombola? Pena Ine kodi ndilibe mphamvu zakupulumutsa? Taona pa kudzudzula kwanga ndiumitsa nyanja, ndi kusandutsa mitsinje chipululu; nsomba zake zinunkha chifukwa mulibe madzi, ndipo zifa ndi ludzu.


Fuula zolimba, usalekerere, kweza mau ako ngati lipenga, ndi kuwafotokozera anthu anga cholakwa chao, ndi banja la Yakobo machimo ao.


Mau anu anapezeka, ndipo ndinawadya; mau anu anakhala kwa ine chikondwero ndi chisangalalo cha mtima wanga; pakuti ndatchedwa dzina lanu, Yehova Mulungu wa makamu.


Tamvani mau a Yehova, iwe nyumba ya Yakobo, ndi inu mabanja onse a nyumba ya Israele;


Wanzeru ndani, kuti azindikire izi? Waluntha, kuti adziwe izi? Pakuti njira za Yehova zili zoongoka; ndipo olungama adzayendamo, koma olakwa adzagwamo.


Tamvanitu ichi, akulu a nyumba ya Yakobo inu, ndi oweruza a nyumba ya Israele inu, akuipidwa nacho chiweruzo, ndi kupotoza zoongoka zonse.


Pamenepo anayankha, nanena kwa ine, ndi kuti, Awa ndi mau a Yehova kwa Zerubabele, Ndi khamu la nkhondo ai, ndi mphamvu ai, koma ndi Mzimu wanga, ati Yehova wa makamu.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kodi dzanja la Mulungu lafupikira? Tsopano udzapenya ngati mau anga adzakuchitikira kapena iai.


Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:


Anayankha nati kwa iye, Atate wathu ndiye Abrahamu. Yesu ananena nao, Ngati muli ana a Abrahamu, mukadachita ntchito za Abrahamu.


Ndipo tsopano chabwino chija chinandikhalira imfa kodi? Msatero ai. Koma uchimo, kuti uoneke kuti uli uchimo, wandichitira imfa mwa chabwino chija; kuti uchimo ukakhale wochimwitsa ndithu mwa lamulo.


Simupsinjika mwa ife, koma mupsinjika mumtima mwanu.


akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa