Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 7:28 - Buku Lopatulika

28 Ndipo panakhala pamene Yesu anatha mau amenewa, makamu a anthu anazizwa ndi chiphunzitso chake:

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

28 Ndipo panakhala pamene Yesu anatha mau amenewa, makamu a anthu anazizwa ndi chiphunzitso chake:

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

28 Yesu atatsiriza kunena zimenezi, anthu onse aja adadabwa ndi kaphunzitsidwe kake,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

28 Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake,

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 7:28
18 Mawu Ofanana  

Inu ndinu wokongola ndithu koposa ana a anthu; anakutsanulirani chisomo pa milomo yanu, chifukwa chake Mulungu anakudalitsani kosatha.


Ndipo panali, pamene Yesu anatha kuwafotokozera ophunzira ake khumi ndi awiri, Iye anachokera kumeneko kukaphunzitsa ndi kulalikira m'mizinda mwao.


Ndipo panali pamene Yesu anatha mau amenewa, anachokera ku Galileya, nadza ku malire a Yudeya, a ku tsidya lija la Yordani.


Ndipo pamene makamu a anthu anamva, anazizwa ndi chiphunzitso chake.


Ndipo panali pamene Yesu anatha mau onse amenewa, anati kwa ophunzira ake,


ndipo inagwa mvula, nidzala mitsinje, ndipo zinaomba mphepo, zinagunda pa nyumbayo; ndipo inagwa; ndi kugwa kwake kunali kwakukulu.


pakuti anawaphunzitsa monga mwini mphamvu, wosanga alembi ao.


Ndipo anazizwa ndi chiphunzitso chake; pakuti anaphunzitsa monga mwini mphamvu, si monga alembi.


Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.


Ndipo pofika tsiku la Sabata, anayamba kuphunzitsa m'sunagoge; ndipo ambiri anamva Iye, nazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti izi? Nzeru yopatsidwa kwa munthuyu njotani, ndi zamphamvu zotere zochitidwa ndi manja ake?


ndipo sanapeze chimene akachita; pakuti anthu onse anamlendewera Iye kuti amve.


Ndipo onse amene anamva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake, ndi mayankho ake.


Ndipo onse anamchitira Iye umboni nazizwa ndi mau a chisomo akutuluka m'kamwa mwake; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?


chifukwa mau ake anali ndi ulamuliro.


Pamene Yesu adamaliza mau ake onse m'makutu a anthu, analowa mu Kapernao.


Chifukwa chake Ayuda anazizwa, nanena, Ameneyu adziwa bwanji zolemba, wosaphunzira?


Anyamatawo anayankha, Nthawi yonse palibe munthu analankhula chotero.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa