Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 26:70 - Buku Lopatulika

70 Koma iye anakana pamaso pa anthu onse, kuti, Chimene unena sindichidziwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

70 Koma iye anakana pamaso pa anthu onse, kuti, Chimene unena sindichidziwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

70 Koma iye adakana pamaso pa anthu onse, adati, “Sindikuzidziŵa zimenezo ine.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

70 Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 26:70
17 Mawu Ofanana  

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.


Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa; koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.


Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.


Ndipo ndi yani amene wamuopa ndi kuchita naye mantha, kuti wanama, osandikumbukira Ine, kapena kundisamalira? Kodi Ine sindinakhale chete nthawi yambiri, ndipo iwe sunandiope Ine konse?


Mtima ndiwo wonyenga koposa, ndi wosachiritsika, ndani angathe kuudziwa?


Ndipo onani, mmodzi wa iwo anali pamodzi ndi Yesu, anatansa dzanja lake, nasolola lupanga lake, nakantha kapolo wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.


Koma izi zonse zinachitidwa, kuti zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.


Koma Petro anamtsata kutali, kufikira kubwalo la mkulu wa ansembe, nalowamo, nakhala pansi ndi anyamata, kuti aone chimaliziro.


Ndipo Petro adakhala pabwalo: ndipo mdzakazi anadza kwa iye, nanena, Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.


Ndipo pamene iye anatuluka kunka kuchipata, mkazi wina anamuona, nati kwa iwo a pomwepo, Uyonso anali ndi Yesu Mnazarayo.


Koma anakana, nati, Mkaziwe, sindimdziwa Iye.


Chabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi chikhulupiriro chako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:


Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.


Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse a mabodza, cholandira chao chidzakhala m'nyanja yotentha ndi moto ndi sulufure; ndiyo imfa yachiwiri.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa