Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 23:7 - Buku Lopatulika

7 ndi kulonjeredwa m'misika, ndi kutchedwa ndi anthu, Rabi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 ndi kulonjeredwa m'misika, ndi kutchedwa ndi anthu, Rabi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Amakondanso kuti anthu aziŵalonjera mwaulemu pa misika, ndipo kuti aziŵatchula aphunzitsi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 23:7
19 Mawu Ofanana  

Koma ndidzafanizira ndi chiyani obadwa awa a makono? Ali ofanana ndi ana akukhala m'mabwalo a malonda, amene alikuitana anzao.


Koma inu musatchedwa Rabi; pakuti Mphunzitsi wanu ali mmodzi, ndipo inu nonse muli abale.


Ndipo Yudasi, womperekayo anayankha nati, Kodi ndine, Rabi? Iye ananena kwa iye, Iwe watero.


Ndipo pomwepo anadza kwa Yesu, nati, Tikuoneni, Rabi; nampsompsonetsa.


Ndipo Yesu anamyankha, nati, Ufuna kuti ndikuchitire chiyani? Ndipo wakhunguyo anati kwa Iye, Raboni, ndilandire kuona kwanga.


Ndipo Petro anakumbukira, nanena naye, Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.


Ndipo m'chiphunzitso chake ananena, Yang'anirani mupewe alembi, akufuna kuyendayenda ovala miinjiro, ndi kulonjeredwa pamisika,


Ndipo atafika, pomwepo anadza kwa Iye, nanena, Rabi; nampsompsonetsa.


Ndipo Petro anayankha, nanena ndi Yesu, Rabi, kutikomera ife kukhala pano; ndipo timange misasa itatu; umodzi wa inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya.


Tsoka inu, Afarisi! Chifukwa mukonda mipando yaulemu m'masunagoge, ndi kupatsidwa moni m'misika.


Koma Yesu anacheuka, napenya iwo alikumtsata, nanena nao, Mufuna chiyani? Ndipo anati kwa Iye, Rabi (ndiko kunena posandulika, Mphunzitsi), mukhala kuti?


Natanaele anayankha Iye, Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu, ndinu mfumu ya Israele.


Ophunzira ananena ndi Iye, Rabi, Ayuda analikufuna kukuponyani miyala tsopano apa; ndipo munkanso komweko kodi?


Yesu ananena naye, Maria. Iyeyu m'mene anacheuka, ananena ndi Iye mu Chihebri, Raboni; chimene chinenedwa, Mphunzitsi.


Iyeyu anadza kwa Yesu usiku, nati kwa Iye, Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu mphunzitsi wochokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kuchita zizindikiro zimene Inu muchita, ngati Mulungu sakhala naye.


Ndipo anadza kwa Yohane, nati kwa iye, Rabi, Iye amene anali ndi inu tsidya lija la Yordani, amene munamchitira umboni, taonani yemweyu abatiza, ndipo anthu onse alinkudza kwa Iye.


Pa mphindikati iyi ophunzira ake anampempha Iye, ndi kunena, Rabi, idyani.


Ndipo pamene anampeza Iye tsidya lina la nyanja, anati kwa Iye, Rabi, munadza kuno liti?


Ndipo ophunzira ake anamfunsa Iye, nanena, Rabi, anachimwa ndani, ameneyo, kapena atate wake ndi amake, kuti anabadwa wosaona?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa