Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 21:6 - Buku Lopatulika

6 Ndipo ophunzirawo anamuka, nachita monga Yesu anawauza;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndipo ophunzirawo anamuka, nachita monga Yesu anawauza;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Tsono ophunzira aja adapitadi nakachita monga momwe Yesu adaaŵalamulira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Ophunzirawo anapita nachita monga Yesu anawalamulira.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 21:6
9 Mawu Ofanana  

Ndipo anamuka Abramu monga Yehova ananena kwa iye, ndipo Loti anamuka pamodzi naye: ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi awiri kudza zisanu, pamene anatuluka mu Harani.


Chotero anachita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu, momwemo anachita.


Ndipo Mose anaona ntchito zonse, ndipo, taonani, adaichita monga Yehova adamuuza, momwemo adachita. Ndipo Mose anawadalitsa.


Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anachita.


Ndipo ndinachita monga momwe anandilamulira, ndinatulutsa akatundu anga usana, ngati a pa ulendo wa kundende, ndi madzulo ndinaboola pakhoma ndi dzanja langa, ndinawatulutsa pali mdima, ndi kuwasenza paphewa panga pamaso pao.


Tauzani mwana wamkazi wa Ziyoni, Taona, mfumu yako idza kwa iwe, wofatsa ndi wokwera pabulu, ndi pa kabulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.


nabwera ndi bulu ndi mwana wake, naika pa iwo zovala zao, nakhala Iye pamenepo.


Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.


Kundichititsa chisoni kuti ndinaika Saulo akhale mfumu; pakuti wabwerera wosanditsata Ine, ndipo sanachite malamulo anga. Ndipo Samuele anakwiya; nalira kwa Yehova usiku wonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa