Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 91:5 - Buku Lopatulika

5 Sudzaopa choopsa cha usiku, kapena muvi wopita usana;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Sudzaopa choopsa cha usiku, kapena muvi wopita usana;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Sudzachita mantha ndi zoopsa zausiku, kapena nkhondo nthaŵi yamasana.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 91:5
19 Mawu Ofanana  

Popeza Ambuye adamvetsa khamu la Aaramu phokoso la magaleta ndi mkokomo wa akavalo, phokoso la nkhondo yaikulu; nanenana wina ndi mnzake, Taonani mfumu ya Israele watimemezera mafumu a Ahiti ndi mafumu a Aejipito, atigwere.


Pakuti mivi ya Wamphamvuyonse yandilowa, mzimu wanga uwumwa ulembe wake; zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.


Sadzaopa mbiri yoipa; mtima wake ngwokhazikika, wokhulupirira Yehova.


Chifukwa chake sitidzachita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja.


Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.


Onsewo agwira lupanga, nazolowera nkhondo: Yense ali ndi lupanga lake pantchafu pake, chifukwa cha upandu wa usiku.


Mtima wanga uguguda, mantha andiopsetsa ine; chizirezire chimene ndinachikhumba chandisandukira kunthunthumira.


Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.


Ndipo ananena Iye kwa iwo, Muli amantha bwanji, okhulupirira pang'ono inu? Pomwepo Iye anauka, nadzudzula mphepo ndi nyanja, ndipo panagwa bata lalikulu.


Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?


Koma zindikirani ichi, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yake yakudza mbala, akadadikira, ndipo sakadalola nyumba yake ibooledwe.


Kotero kuti tinena molimbika mtima, Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa; adzandichitira chiyani munthu?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa