Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 9:5 - Buku Lopatulika

5 Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo, mwafafaniza dzina lao kunthawi yonka muyaya.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo, mwafafaniza dzina lao kunthawi yonka muyaya.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Mwaimba mlandu mafuko a anthu, mwaononga anthu oipa. Adzaiŵalika mpaka muyaya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 9:5
24 Mawu Ofanana  

Ndipo Ahitofele, pakuona kuti sautsata uphungu wake anamanga bulu wake, nanyamuka, nanka kumzinda kwao, nakonza za pa banja lake, nadzipachika, nafa, naikidwa m'manda a atate wake.


kubwezera chilango akunja, ndi kulanga mitundu ya anthu;


Aphokoseranji amitundu, nalingiriranji anthu zopanda pake?


Mudzaononga iwo akunena bodza; munthu wokhetsa mwazi ndi wachinyengo, Yehova anyansidwa naye.


Akapanda kutembenuka munthu, iye adzanola lupanga lake; wakoka uta wake, naupiringidza.


Ndipo anapirikitsa amitundu pamaso pao, nawagawira cholowa chao, ndi muyeso, nakhalitsa mafuko a Israele m'mahema mwao.


Anenerenji amitundu, Ali kuti Mulungu wao? Kubwezera chilango cha mwazi wa atumiki anu umene anaukhetsa kudziwike pakati pa amitundu pamaso pathu.


Amayesa wolungama wodala pomkumbukira; koma dzina la oipa lidzavunda.


Kuunika kwa olungama kukondwa; koma nyali ya oipa idzazima.


ndipo ndidzaika mpando wachifumu wanga mu Elamu, ndipo ndidzaononga pamenepo mfumu ndi akulu, ati Yehova.


Ambuye munanenera moyo wanga milandu yake; munaombola moyo wanga.


Ndipo mudzapondereza oipa; pakuti adzakhala ngati mapulusa kumapazi anu, tsiku ndidzaikalo, ati Yehova wa makamu.


undileke, ndiwaononge, ndi kufafaniza dzina lao pansi pa thambo; ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi waukulu woposa iwo.


Ndipo m'kamwa mwake mutuluka lupanga lakuthwa, kuti akanthe nalo mitundu ya anthu; ndipo Iye adzawalamulira ndi ndodo yachitsulo: ndipo aponda Iye moponderamo mphesa mwa vinyo waukali wa mkwiyo wa Mulungu Wamphamvuyonse.


Ndipo Davide anati kwa Abigaile, Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israele, amene anakutumiza lero kudzandichingamira ine;


Ndipo pamene Davide anamva kuti Nabala adamwalira, iye anati, Alemekezedwe Yehova, amene anaweruza mlandu wa mtonzo wanga wochokera ku dzanja la Nabala, naletsa mnyamata wake pa choipa; ndipo Yehova anabwezera pamutu pa Nabala choipa chake. Ndipo Davide anatumiza wokamfunsira Abigaile, zakuti amtengere akhale mkazi wake.


Tsono Saulo ananena ndi wonyamula zida zake, Solola lupanga lako, undipyoze nalo; kuti osadulidwa awa angabwere ndi kundipyoza, ndi kundiseka. Koma wonyamula zida zake anakana; chifukwa anaopa ndithu. Chifukwa chake Saulo anatenga lupanga lake naligwera.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa