Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 79:6 - Buku Lopatulika

6 Thirirani mkwiyo wanu pa akunja osadziwa Inu, ndi pa maufumu osaitana pa dzina lanu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Thirirani mkwiyo wanu pa akunja osadziwa Inu, ndi pa maufumu osaitana pa dzina lanu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Gwetsani ukali wanu pa mitundu ya anthu osakudziŵani, ndiponso pa maufumu osatama dzina lanu mopemba.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 79:6
22 Mawu Ofanana  

Kodi onse ochita zopanda pake sadziwa kanthu? Pakudya anthu anga monga akudya mkate, ndipo saitana pa Yehova.


Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, onse akuitanira kwa Iye m'choonadi.


Kodi ochita zopanda pake sadziwa? Pomadya anthu anga monga akudya mkate; ndipo saitana Mulungu.


Muwatsanulire mkwiyo wanu, ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.


Chifukwa chake anatsanulira pa iye mkwiyo wake waukali, ndi mphamvu za nkhondo; ndipo unamyatsira moto kuzungulira kwake, koma iye sanadziwe; ndipo unamtentha, koma iye sanachisunge m'mtima.


Tsanulirani ukali wanu pa amitundu osakudziwani Inu, ndi pa mabanja osaitana dzina lanu; pakuti anadya Yakobo, inde, anamudya namutha, napasula mokhalamo mwake.


Pakuti, taonani, ndiyamba kuchita choipa pa mzinda umene utchedwa ndi dzina langa, kodi inu mudzakhala osalangidwa konse? Simudzakhala osalangidwa; pakuti ndidzaitana lupanga ligwe pa onse okhala m'dziko lapansi, ati Yehova wa makamu.


Chifukwa chake, mundilindire, ati Yehova, kufikira tsiku loukira Ine zofunkha; pakuti ndatsimikiza mtima Ine kusonkhanitsa amitundu, kuti ndimemeze maufumu kuwatsanulira kulunda kwanga, ndilo mkwiyo wanga wonse waukali; pakuti dziko lonse lapansi lidzathedwa ndi moto wa nsanje yanga.


Ndipo izi adzachita, chifukwa sanadziwe Atate, kapena Ine.


Atate wolungama, dziko lapansi silinadziwe Inu, koma Ine ndinadziwa Inu; ndipo iwo anazindikira kuti munandituma Ine;


Pakuti popita, ndi kuona zinthu zimene muzipembedza, ndipezanso guwa la nsembe lolembedwa potere, KWA MULUNGU WOSADZIWIKA. Chimene muchipembedza osachidziwa, chimenecho ndichilalikira kwa inu.


Ndipo monga iwo anakana kukhala naye Mulungu m'chidziwitso chao, anawapereka Mulungu kumtima wokanika, kukachita zinthu zosayenera;


kwa Mpingo wa Mulungu wakukhala mu Korinto, ndiwo oyeretsedwa mwa Khristu Yesu, oitanidwa akhale oyera mtima, pamodzi ndi onse akuitana pa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, m'malo monse, ndiye wao, ndi wathu:


m'lawi lamoto, ndi kubwezera chilango kwa iwo osamdziwa Mulungu, ndi iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Ambuye wathu Yesu;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa