Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 68:10 - Buku Lopatulika

10 Gulu lanu linakhala m'dziko muja. Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Gulu lanu linakhala m'dziko muja. Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Anthu anu adapezamo malo okhala. Inu Mulungu, mudapatsa anthu osauka zosoŵa zao mwa ubwino wanu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 68:10
18 Mawu Ofanana  

pamenepo mverani Inu mu Mwamba, ndi kukhululukira tchimo la akapolo anu, ndi la anthu anu Aisraele; pakuti muwaphunzitsa njira yokoma ayenera kuyendamo, ndi kupatsa mvula padziko lanu, limene munawapatsa anthu anu likhale cholowa chao.


Mukhutitsa nthaka yake yolima; mufafaniza nthumbira zake; muiolowetsa ndi mvumbi; mudalitsa mmera wake.


Muveka chakachi ndi ukoma wanu; ndipo mabande anu akukha zakucha.


Mucheza nalo dziko lapansi, mulithirira, mulilemeretsa kwambiri; mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi, muwameretsera tirigu m'mene munakonzera nthaka.


Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa chilombo; musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.


Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendako ndi mitsinje inasefuka; kodi adzakhozanso kupatsa mkate? Kodi adzafunira anthu ake nyama?


Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye ameme alibe mphamvu.


Ndipo anasonkhana motsutsana pa Mose ndi Aroni, nanena nao, Mukula mphamvu inu, pakuti khamu lonse nlopatulika, onsewa, ndipo Yehova ali pakati pao; mudzikuza bwanji pa msonkhano wa Yehova?


akhungu alandira kuona kwao, ndi opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ndi ogontha akumva, ndi akufa aukitsidwa, ndi kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.


Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino, ndipo eni chuma anawachotsa opanda kanthu.


Ndipo muyankhe ndi kuti pamaso pa Yehova Mulungu wanu, Kholo langa ndiye Mwaramu wakuti atayike, natsika kunka ku Ejipito, nagoneragonera komweko ali nao anthu pang'ono, nasandukako mtundu waukulu, wamphamvu, ndi wochuluka anthu ake;


osati monga ochita ufumu pa iwo a udindo wanu, koma okhala zitsanzo za gululo.


Amuutsa waumphawi m'fumbi, nanyamula wosowa padzala, kukamkhalitsa kwa akalonga; ndi kuti akhale nacho cholowa cha chimpando cha ulemerero. Chifukwa nsanamira za dziko lapansi nza Yehova, ndipo Iye anakhazika dziko pa izo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa