Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 46:3 - Buku Lopatulika

3 Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 ngakhale nyanja zikokome ndi kututuma. Ngakhale mapiri anjenjemere ndi kulindima kwa nyanja.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu, ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 46:3
17 Mawu Ofanana  

Ndipo Iye anati, Tuluka, nuime paphiri lino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikulu ndi yamphamvu inang'amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhale m'mphepomo. Itapita mphepoyo kunali chivomezi; komanso Yehova sanali m'chivomezicho.


ndi kuti, Ufike mpaka apa, osapitirirapo; apa adzaletseka mafunde ako odzikuza?


Zingwe za imfa zinandizinga, ndipo mitsinje ya zopanda pake inandiopsa.


Ndipo tsopano, inu okhala mu Yerusalemu, ndi anthu a Yuda, weruzanitu mlandu wa ine ndi munda wanga wampesa.


Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.


Ndinaona mapiri, taona ananthunthumira; ndipo zitunda zonse zinagwedezeka.


Kodi simundiopa Ine? Ati Yehova: simudzanthunthumira pamaso pa Ine, amene ndinaika mchenga chilekaniro cha nyanja, ndi lemba lamuyaya kuti isapitirirepo? Ndipo ngakhale mafunde ake achita gavigavi, alephera; ngakhale akokoma, sangathe kupitirirapo.


Ndi mapiri adzasungunuka pansi pa Iye, ndi zigwa zidzang'ambika, ngati sera pamoto, ngati madzi otsanulidwa potsetsereka.


Mapiri agwedezeka chifukwa cha Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pake, ndi maiko ndi onse okhala m'mwemo.


ndipo inagwa mvula, nidzala mitsinje, ndipo zinaomba mphepo, zinagunda pa nyumbayo; koma siinagwe; chifukwa inakhazikika pathanthwepo.


Ndipo zisumbu zonse zidathawa, ndi mapiri sanapezeke.


Ndipo anena ndi ine, Madziwo udawaona uko akhalako mkazi wachigololoyo ndiwo anthu, ndi makamu, ndi mitundu, ndi manenedwe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa