Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 44:10 - Buku Lopatulika

10 Mutibwereretsa kuthawa otisautsa, ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Mutibwereretsa kuthawa otisautsa, ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Mwalola kuti amaliwongo athu atipirikitse, ndipo adani athu apeza zofunkha kwathu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 44:10
19 Mawu Ofanana  

Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima, ndipo Iye adzapondereza otisautsa.


Munakaniza chipangano cha mtumiki wanu; munaipsa korona wake ndi kumponya pansi.


Onse opita panjirapa amfunkhira, akhala chotonza cha anansi ake.


Munapinditsa kukamwa kwake kwa lupanga lake, osamuimika kunkhondo.


dzanja langa lapeza monga chisa, chuma cha mitundu ya anthu, ndipo monga munthu asonkhanitsa mazira osiyidwa, ine ndasonkhanitsa dziko lonse lapansi, ndipo panalibe chogwedeza phiko, kapena chotsegula pakamwa, kapena cholira pyepye.


Ine ndidzamtumiza kumenyana ndi mtundu wosalemekeza, ndi pa anthu a mkwiyo wanga ndidzamlangiza, kuti afunkhe, agwire zolanda, awapondereze pansi, monga dothi la pamakwalala.


Chuma chako ndi zosungidwa zako ndidzazipereka zifunkhidwe kopanda mtengo wake, ichicho chidzakugwera chifukwa cha zochimwa zako zonse, m'malire ako onse.


Pakuti paliponse ndinena, ndifuula; ndifuula, Chiwawa ndi chofunkha; pakuti mau a Yehova ayesedwa kwa ine chitonzo, ndi choseketsa, dzuwa lonse.


Koma mukapanda kundimvera Ine, osachita malamulo awa onse;


Ndipo nkhope yanga idzatsutsana nanu; kuti adani anu adzakukanthani, ndipo akudana ndi inu adzachita ufumu pa inu ndipo mudzathawa wopanda wakukulondolani.


Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.


Pakuti Aamaleke ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, chifukwa chake Yehova sadzakhala nanu.


Yehova adzalola adani anu akukantheni; mudzawatulukira njira imodzi, koma mudzawathawa pamaso pao njira zisanu ndi ziwiri, ndipo mudzagwedezeka pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.


Pamenepo ndidzawapsera mtima tsiku ilo, ndipo ndidzawataya, ndi kuwabisira nkhope yanga, ndipo adzathedwa, ndi zoipa ndi zovuta zambiri zidzawafikira; kotero kuti adzati tsiku lija, Sizitifikira kodi zoipa izi popeza Mulungu wathu sakhala pakati pa ife?


Mwa ichi ana a Israele sangathe kuima pamaso pa adani ao, awafulatira adani ao, pakuti aperekedwa aonongeke. Sindidzakhalanso nanu mukapanda kuononga choperekedwacho, kuchichotsa pakati pa inu.


Ndidzanenanji, Ambuye, Israele atabwerera m'mbuyo pamaso pa adani ao?


Ndipo wakubwera ndi mauyo anayankha, nati, Israele anathawa pamaso pa Afilisti, ndiponso kunali kuwapha kwakukulu kwa anthu, ndi ana anu awiri omwe Hofeni ndi Finehasi afa, ndipo likasa la Mulungu lalandidwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa