Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 38:10 - Buku Lopatulika

10 Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yachoka, ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandichokera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yachoka, ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandichokera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zandithera, ndipo sindikutha kupenya bwino.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 38:10
12 Mawu Ofanana  

Maso anga anatha mphamvu pofuna chipulumutso chanu, ndi mau a chilungamo chanu.


Pakuti moyo wanga watha ndi chisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo. Mphamvu yanga yafooka chifukwa cha kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.


Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje; motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.


Lapuwala diso langa chifukwa cha chisoni; lakalamba chifukwa cha onse akundisautsa.


Ndalema ndi kufuula kwanga; kum'mero kwauma gwaa! M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.


Diso langa lapuwala chifukwa cha kuzunzika kwanga: Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse; nditambalitsira manja anga kwa Inu.


Mtima wanga uguguda, mantha andiopsetsa ine; chizirezire chimene ndinachikhumba chandisandukira kunthunthumira.


Maso anga alefuka ndi misozi, m'kati mwanga mugwedezeka; chiwindi changa chagwa pansi chifukwa cha kupasuka kwa mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga; chifukwa tiana ndi oyamwa akomoka m'makwalala a mzindawu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa