Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 23:2 - Buku Lopatulika

2 Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Amandigoneka pa busa lamsipu. Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Amandigoneka pa msipu wobiriwira, amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 23:2
11 Mawu Ofanana  

Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani? Akabisa nkhope yake adzampenyerera ndani? Chikachitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, nchimodzimodzi;


Pali mtsinje, ngalande zake zidzakondweretsa mzinda wa Mulungu. Malo oyera okhalamo Wam'mwambamwamba.


Ndipo anafika pa Elimu, ndi pamenepo panali akasupe a madzi khumi ndi awiri, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; ndipo anamanga chigono chao pomwepo pamadziwo.


Ndipo Mulungu adzapatsa mvula ya mbeu yako, ukaibzale m'nthaka; ndi mkate ndiwo phindu la nthaka, ndipo tirigu wake adzacha bwino ndi kuchuluka; tsiku limenelo ng'ombe zako zidzadya m'madambo aakulu.


Popeza anthu awa akana madzi a Siloamu, amene ayenda pang'onopang'ono, nakondwerera mwa Rezini ndi mwa mwana wa Remaliya;


Ndipo anati kwa ine, Zatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa iye wakumva ludzu ndidzampatsa amwe kukasupe wa madzi a moyo kwaulere.


Ndipo anandionetsa mtsinje wa madzi a moyo, wonyezimira ngati krustalo, otuluka kumpando wachifumu wa Mulungu ndi wa Mwanawankhosa.


Ndipo Mzimu ndi mkwatibwi anena, Idzani. Ndipo wakumva anene, Idzani. Ndipo wakumva ludzu adze; iye wofuna, atenge madzi a moyo kwaulere.


chifukwa Mwanawankhosa wakukhala pakati pa mpando wachifumu adzawaweta, nadzawatsogolera ku akasupe a madzi amoyo, ndipo Mulungu adzawapukutira misozi yonse pamaso pao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa