Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 137:9 - Buku Lopatulika

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako, ndi kuwaphwanya pathanthwe.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako, ndi kuwaphwanya pathanthwe.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Adzakhala wodala munthu amene adzatenga makanda ako ndi kuŵakankhanthitsa ku thanthwe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 137:9
5 Mawu Ofanana  

Nati Hazaele, Muliriranji, mbuye wanga? Nayankha iye, Popeza ndidziwa choipa udzachitira ana a Israele; udzatentha malinga ao ndi moto, nudzapha anyamata ao ndi lupanga, nudzaphwanya makanda ao, nudzang'amba akazi ao okhala ndi pakati.


Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.


Momwemo phokoso lidzaukira anthu ako, ndi malinga ako onse adzapasuka, monga Salimani anapasula Betaribele; tsiku la nkhondo amai anaphwanyika pamodzi ndi ana ake.


Samariya adzasanduka wabwinja, pakuti anapandukana ndi Mulungu wake; iwo adzagwa ndi lupanga, ana ao amakanda adzaphwanyika, ndi akazi ao okhala ndi pakati adzatumbulidwa.


Koma iye anatengedwa, analowa ndende; ana ake a makanda anaphwanyika polekeza pake pa miseu yake yonse; ndi pa omveka ake anachita maere, ndi akulu ake onse anamangidwa maunyolo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa