Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 10:16 - Buku Lopatulika

16 Yehova ndiye Mfumu kunthawi yamuyaya; aonongeka amitundu m'dziko lake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Yehova ndiye Mfumu kunthawi yamuyaya; aonongeka amitundu m'dziko lake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Chauta ndiye Mfumu mpaka muyaya. Mitundu ya anthu akunja idzatheratu m'dziko lake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 10:16
20 Mawu Ofanana  

Ukulu, ndi mphamvu, ndi ulemerero, ndi chipambano, ndi chifumu ndi zanu, Yehova; pakuti zonse zam'mwamba ndi padziko lapansi ndi zanu; ufumu ndi wanu, Yehova; ndipo mwakwezeka mutu wa pa zonse.


Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya, ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonseyonse.


Yehova adzachita ufumu kosatha, Mulungu wako, Ziyoni, ku mibadwomibadwo. Aleluya.


Yehova anakhala pa chigumula, inde Yehova akhala mfumu kunthawi yonka muyaya.


Ndipo anapirikitsa amitundu pamaso pao, nawagawira cholowa chao, ndi muyeso, nakhalitsa mafuko a Israele m'mahema mwao.


Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba, lakodwa phazi lao muukonde anautchera.


Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo, mwafafaniza dzina lao kunthawi yonka muyaya.


Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m'chilungamo, nadzaweruza anthu molunjika.


Yehova achita ufumu; wadziveka ndi ukulu; wadziveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m'chuuno; dziko lomwe lokhalamo anthu likhakizika, silidzagwedezeka.


Yehova adzachita ufumu nthawi yonka muyaya.


Pakuti Yehova ndiye woweruza wathu, Yehova ndiye wotipatsa malamulo, Yehova ndiye mfumu yathu; Iye adzatipulumutsa.


Koma Yehova ndiye Mulungu woona; ndiye Mulungu wamoyo, mfumu yamuyaya; pa mkwiyo wake dziko lapansi lidzanthunthumira, ndi amitundu sangapirire ukali wake.


Inu, Yehova, mukhala chikhalire, ndi mpando wanu wachifumu ku mibadwomibadwo.


Atatha masiku awa tsono, ine Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndi nzeru zanga zinandibwerera; ndipo ndinalemekeza Wam'mwambamwamba, ndi kumyamika ndi kumchitira ulemu Iye wokhala chikhalire; pakuti kulamulira kwake ndiko kulamulira kosatha, ndi ufumu wake ku mibadwomibadwo;


Ndilamulira ine kuti m'maiko onse a ufumu wanga anthu anjenjemere, naope pamaso pa Mulungu wa Daniele; pakuti Iye ndiye Mulungu wamoyo wakukhala chikhalire, ndi ufumu wake ngwosaonongeka, ndi kulamulira kwake kudzakhala mpaka chimaliziro.


Monga amitundu amene Yehova awaononga pamaso panu, momwemo mudzaonongeka; chifukwa cha kusamvera mau a Yehova Mulungu wanu.


Ndipo kwa Mfumu yosatha, yosavunda, yosaoneka, Mulungu wa yekha, ukhale ulemu ndi ulemerero, kufikira nthawi za nthawi. Amen.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa