Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 1:1 - Buku Lopatulika

1 Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa, kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa, kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Ngwodala munthu wosatsata uphungu wa anthu oipa, wosatsanzira mayendedwe a anthu ochimwa, wosakhala nawo m'gulu la anthu onyoza Mulungu,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 1:1
52 Mawu Ofanana  

Mtima wangawe, usalowe mu chiungwe chao; ulemerero wanga, usadziphatike pa msonkhano yao; chifukwa m'kukwiya kwao anapha munthu. M'kufuna kwao anapundula ng'ombe.


ndipo Enoki anayendabe ndi Mulungu; ndipo panalibe iye; pakuti Mulungu anamtenga.


Ndipo kunali monga ngati kunamchepera kuyenda m'machimo a Yerobowamu mwana wa Nebati, iye anakwatira Yezebele mwana wamkazi wa Etibaala mfumu ya Asidoni, natumikira Baala, namgwadira.


Iyenso anayenda m'njira za nyumba ya Ahabu; pakuti wompangira ndi make achite choipa.


Chikukomerani kodi kungosautsa, kuti mupeputsa ntchito yolemetsa manja anu, ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?


Taonani, zokoma zao sizili m'dzanja lao; (koma uphungu wa oipa unditalikira.)


Ngati ndinayanjana nalo bodza, ndi phazi langa linathamangira chinyengo;


Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; koma mayendedwe a oipa adzatayika.


Odala iwo amene asunga chiweruzo, iye amene achita chilungamo nthawi zonse.


Aleluya. Wodala munthu wakuopa Yehova, wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.


Mundichokere ochita zoipa inu; kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.


Odala anthu akuona zotere; odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.


Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize, chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.


Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.


Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wake. Odala onse akumkhulupirira Iye.


Phazi langa liponda pachidikha, m'misonkhano ndidzalemekeza Yehova.


Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino; wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.


Alingirira zopanda pake pakama pake; adziika panjira posati pabwino; choipa saipidwa nacho.


Ndibiseni pa upo wachinsinsi wa ochita zoipa; pa phokoso la ochita zopanda pake.


Potero ndinawaperekera kuuma mtima kwao, ayende monga mwa uphungu waowao.


Yehova wa makamu, wodala munthu wakukhulupirira Inu.


Mwananga, usayende nao m'njira; letsa phazi lako ku mayendedwe ao;


Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?


Nzeru yabwino ipatsa chisomo; koma njira ya achiwembu ili makolokoto.


Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.


Akonzera onyoza chiweruzo, ndi mikwingwirima pamsana pa opusa.


kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota;


Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo.


Njira ya oipa ikunga mdima; sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.


Ukakhala wanzeru, si yakoyako nzeruyo? Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.


Sindinakhala m'msonkhano wa iwo amene asekerasekera, ndi kusangalala; ndinakhala pandekha chifukwa cha dzanja lanu; pakuti mwandidzaza ndi mkwiyo.


Wodala munthu amene akhulupirira Yehova, amene chikhulupiriro chake ndi Yehova.


Ndipo ndinati kwa ana ao m'chipululu, Musamayenda m'malemba a atate anu, musawasunga maweruzo ao, kapena kudzidetsa ndi mafano ao;


Ndipo Yesu anayankha iye, nati, Ndiwe wodala, Simoni Bara-Yona: pakuti thupi ndi mwazi sizinakuululire ichi, koma Atate wanga wa Kumwamba.


Koma Iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.


(amene sanavomereze kuweruza kwao ndi ntchito yao) wa ku Arimatea, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,


Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.


Yesu ananena kwa iye, Chifukwa wandiona Ine, wakhulupirira; odala iwo akukhulupirira, angakhale sanaone.


amene ife tikhoza kulowa naye ndi chikhulupiriro m'chisomo ichi m'mene tilikuimamo; ndipo tikondwera m'chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.


Mwa ichi mudzitengere zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoza kuima chitsutsire pofika tsiku loipa, ndipo, mutachita zonse, mudzachilimika.


Ndipo nyama iliyonse yogawanika chiboda, nikhala yogawanikadi chiboda, nibzikula, imeneyo muyenera kudya.


Wodala iwe, Israele; akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova, ndiye chikopa cha thandizo lako, Iye amene akhala lupanga la ukulu wako! Ndi adani ako adzakugonjera; ndipo udzaponda pa misanje yao.


Pakuti nthawi yapitayi idakufikirani kuchita chifuniro cha amitundu, poyendayenda inu m'kukhumba zonyansa, zilakolako, maledzero, madyerero, maimwaimwa, ndi kupembedza mafano kosaloleka;


Odala iwo amene atsuka miinjiro yao, kuti akakhale nao ulamuliro pa mtengo wa moyo, ndi kuti akalowe m'mzinda pazipata.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa