Maliro 1:9 - Buku Lopatulika9 Udyo wake unali m'nsalu zake; sunakumbukire chitsiriziro chake; chifukwa chake watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza; taonani, Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuza yekha. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20149 Udyo wake unali m'nsalu zake; sunakumbukira chitsiriziro chake; chifukwa chake watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza; taonani, Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuza yekha. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa9 Uve wake unkaonekera poyera, iye osaganizako za tsoka lake lakutsogolo. Nchifukwa chake kugwa kwake kunali koopsa, ndipo panalibe womuthuzitsa mtima. Akungoti, “Inu Chauta, muyang'ane mavuto anga, pakuti adani anga apambana.” Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero9 Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.” Onani mutuwo |
Ndipo tsono, Mulungu wathu, ndinu Mulungu wamkulu, ndi wamphamvu, ndi woopsa, wakusunga pangano ndi chifundo, asachepe pamaso panu mavuto athu onse amene anatigwera ife, ndi mafumu athu, akulu athu, ndi ansembe athu, ndi aneneri athu, ndi makolo athu, ndi anthu anu onse, kuyambira masiku a mafumu a Asiriya, mpaka lero lino.