Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 6:30 - Buku Lopatulika

30 Munthu aliyense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

30 Munthu aliyense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

30 Munthu akakupempha kanthu, uzimpatsa. Ndipo munthu akatenga zinthu zako, usamlamule kuti abweze.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

30 Mupatseni aliyense amene akupemphani kanthu ndipo ngati wina atenga chinthu chanu, musamulamule kuti akubwezereni.

Onani mutuwo Koperani




Luka 6:30
29 Mawu Ofanana  

Anagawagawa, anapatsa aumphawi; chilungamo chake chikhalitsa kosatha; nyanga yake idzakwezeka ndi ulemu.


Wodala iye amene asamalira wosauka! Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa.


Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.


Ena asirira modukidwa tsiku lonse; koma wolungama amapatsa osamana.


Mwini diso lamataya adzadala; pakuti apatsa osauka zakudya zake.


Gawira asanu ndi awiri ngakhale asanu ndi atatu; pakuti sudziwa choipa chanji chidzaoneka pansi pano.


Pompo ndinapereka mtima wanga kudziwa nzeru, ndi kupenya ntchito zichitidwa pansi pano; kuti anthu saona tulo konse ndi maso ao ngakhale usana ngakhale usiku;


Chomwechonso Atate wanga a Kumwamba adzachitira inu, ngati inu simukhululukira yense mbale wake ndi mitima yanu.


koma ndinena kwa inu, Musakanize munthu woipa; koma amene adzakupanda iwe pa tsaya lako lamanja, umtembenuzire linanso.


Ndipo mutikhululukire mangawa athu, monga ifenso takhululukira amangawa anthu.


Koma patsani mphatso yachifundo za m'katimo; ndipo onani, zonse zili zoyera kwa inu.


Gulitsani zinthu muli nazo, nimupatse mphatso zachifundo; mudzikonzere matumba a ndalama amene sakutha, chuma chosatha mu Mwamba, kumene mbala siziyandikira, ndipo njenjete siziononga.


Koma m'mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa chinthu chimodzi: gulitsa zilizonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala nacho chuma chenicheni mu Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.


Iye amene akupanda iwe pa tsaya limodzi umpatsenso linzake; ndi iye amene alanda chofunda chako, usamkanize malaya ako.


Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakuchitirani inu, muwachitire iwo motero inu momwe.


Patsani, ndipo kudzapatsidwa kwa inu; muyeso wabwino, wotsendereka, wokuchumuka, wosefukira, anthu adzakupatsani m'manja mwanu. Pakuti kudzayesedwa kwa inu ndi muyeso womwewo muyesa nao inu.


M'zinthu zonse ndinakupatsani chitsanzo, chakuti pogwiritsa ntchito, kotero muyenera kuthandiza ofooka ndi kukumbuka mau a Ambuye Yesu, kuti anati yekha, Kupatsa kutidalitsa koposa kulandira.


Pakuti mudziwa chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti, chifukwa cha inu anakhala wosauka, angakhale anali wolemera, kuti inu ndi kusauka kwake mukakhale olemera.


Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa