Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 1:73 - Buku Lopatulika

73 chilumbiro chimene Iye anachilumbira kwa Abrahamu atate wathu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

73 chilumbiro chimene Iye anachilumbira kwa Abrahamu atate wathu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

73 Adalonjezanso Abrahamu, kholo lathu, molumbira,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

73 lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:

Onani mutuwo Koperani




Luka 1:73
10 Mawu Ofanana  

Yehova Mulungu wa Kumwamba, amene ananditenga ine kunyumba ya atate wanga, ku dziko la abale anga, amene ananena ndi ine, amene analumbirira ine kuti, Ndidzapatsa mbeu zako dziko ili; Iye adzatumiza mthenga wake akutsogolere, ndipo udzamtengere mwana wanga mkazi kumeneko.


khala mlendo m'dziko muno, ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndipo ndidzadalitsa iwe chifukwa kuti ndidzakupatsa iwe ndi mbeu zako maiko onse awa, ndipo ndidzalimbikitsa chilumbiriro ndinachilumbirira kwa Abrahamu atate wako;


chipanganocho anapangana ndi Abrahamu, ndi lumbiro lake ndi Isaki;


kuti ndikalimbikitse lumbiro limene ndinalumbirira makolo anu, ndiwapatse dziko moyenda mkaka ndi uchi, monga lero lomwe. Ndipo ndinayankha, ndi kuti, Amen, Yehova.


Kutipatsa ife kuti titalanditsidwa kudzanja la adani athu, tidzamtumikira Iye, opanda mantha,


Ndipo kudzakhala, chifukwa cha kumvera inu maweruzo awa, ndi kuwasunga, ndi kuwachita, Yehova Mulungu wanu adzakusungirani chipangano ndi chifundo chimene analumbirira makolo anu;


koma Yehova anakutulutsani ndi dzanja lamphamvu, ndi kukuombolani m'nyumba ya ukapolo, m'dzanja la Farao mfumu ya Aejipito, chifukwa Yehova akukondani, ndi chifukwa cha kusunga lumbiro lija analumbirira makolo anu.


Pakuti pamene Mulungu analonjezana naye Abrahamu, popeza analibe wamkulu woposa kumlumbira, analumbira pa Iye yekha,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa