Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 1:72 - Buku Lopatulika

72 Kuchitira atate athu chifundo, ndi kukumbukira pangano lake lopatulika;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

72 Kuchitira atate athu chifundo, ndi kukumbukira pangano lake lopatulika;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

72 Choncho Iye waŵachitiradi chifundo makolo athu akale, ndipo wakumbukira chipangano chake choyera.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

72 kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,

Onani mutuwo Koperani




Luka 1:72
21 Mawu Ofanana  

ndipo ndidzadalitsa amene akudalitsa iwe; ndi kutemberera iye amene akutemberera iwe; ndipo mwa iwe adzadalitsidwa mabanja onse a dziko lapansi.


m'mbeu zako mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsidwa: chifukwa wamvera mau anga.


ndipo ndidzachulukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, ndipo ndidzapatsa mbeu zako maiko onsewa; m'mbeu zako mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsidwa;


mbeu zako zidzakhala monga fumbi lapansi, ndipo udzabalalikira kumadzulo ndi kum'mawa ndi kumpoto ndi kumwera: mwa iwe ndi mu mbeu zako mabanja onse a dziko lapansi adzadalitsidwa.


chipanganocho anapangana ndi Abrahamu, ndi lumbiro lake ndi Isaki;


Popeza anakumbukira mau ake oyera, ndi Abrahamu mtumiki wake.


Ndipo anawakumbukira chipangano chake, naleza monga mwa kuchuluka kwa chifundo chake.


Anapatsa akumuopa Iye chakudya; adzakumbukira chipangano chake kosatha.


Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake kunyumba ya Israele; malekezero onse a dziko lapansi anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.


Koma ndidzakumbukira Ine pangano langa ndi iwe m'masiku a ubwana wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha nawe.


Ndipo popita Ine panali iwepo ndi kukupenya, taona nyengo yako ndiyo nyengo yakukondana; pamenepo ndinakufunda chofunda changa, ndi kuphimba umaliseche wako; inde ndinakulumbirira ndi kupangana nawe, ati Ambuye Yehova, ndipo unakhala wanga.


pamenepo ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo; ndiponso pangano langa ndi Isaki, ndiponso pangano langa ndi Abrahamu ndidzakumbukira; ndipo ndidzakumbukira dzikoli.


Mudzapatsa kwa Yakobo choonadi, ndi kwa Abrahamu chifundo chimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.


Kunena za Uthenga Wabwino, iwo ali ngati adani, chifukwa cha inu; koma kunena za chisankhidwe, ali okondedwa, chifukwa cha makolo.


ndiwo Aisraele; ali nao umwana, ndi ulemerero, ndi mapangano, ndi kupatsa kwa malamulo, ndi kutumikira mu Kachisi wa Mulungu, ndi malonjezo;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa