Hoseya 9:4 - Buku Lopatulika4 Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa achisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m'nyumba ya Yehova. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20144 Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa achisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m'nyumba ya Yehova. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa4 Kumeneko anthu sadzaperekanso zopereka za chakumwa kupereka kwa Chauta. Sadzamkondwetsanso ndi nsembe zao. Chakudya chao chidzakhala ngati chakudya chapamaliro, onse amene adzadya chakudya chimenecho adzaipitsidwa. Chakudyacho chidzangokhala chodyera njala chabe, osati choti nkukapereka ku Nyumba ya Chauta. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova. Onani mutuwo |