Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 9:21 - Buku Lopatulika

21 namwa vinyo wake, naledzera; ndipo anali wamaliseche m'kati mwa hema wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 namwa vinyo wake, naledzera; ndipo anali wamaliseche m'kati mwa hema wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Tsiku lina atangomwa vinyo, adaledzera, ndipo adavula zovala zake zonse, nakagona ali maliseche m'hema mwake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 9:21
13 Mawu Ofanana  

Mibadwo ya Nowa ndi iyi: Nowa anali munthu wolungama ndi wangwiro m'mibadwo yake; Nowa anayendabe ndi Mulungu.


Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wampesa:


Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa; wosochera nazo alibe nzeru.


Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene achita zabwino osachimwa.


Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.


Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.


njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.


okalamba akhale odzisunga, olemekezeka, odziletsa, olama m'chikhulupiriro, m'chikondi, m'chipiriro.


ndikulangiza ugule kwa Ine golide woyengeka m'moto, kuti ukakhale wachuma, ndi zovala zoyera, kuti ukadziveke, ndi kuti manyazi a usiwa wako asaoneke; ndi mankhwala opaka m'maso mwako, kuti ukaone.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa