Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 34:25 - Buku Lopatulika

25 Ndipo panali tsiku lachitatu pamene anamva kuwawa, ana aamuna awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, abale ake a Dina, anatenga wina lupanga lake wina lake, nalimbika mtima nalowa m'mzinda napha amuna onse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

25 Ndipo panali tsiku lachitatu pamene anamva kuwawa, ana amuna awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, abale ake a Dina, anatenga wina lupanga lake wina lake, nalimbika mtima nalowa m'mudzi napha amuna onse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

25 Patangopita masiku atatu, zilonda za kuumbala kuja zisanapole pa anthu aja, ana aŵiri a Yakobe, Simeoni ndi Levi, alongo ake a Dina, adatenga mikondo yao, nakaloŵa mosadziŵika mumzinda muja, nkukapha amuna onse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

25 Patapita masiku atatu, amuna onse akumvabe ululu wa kuchita mdulidwe uja, ana awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, alongo ake a Dina, anatenga malupanga ndi kulowa mu mzindawo mwakachetechete napha amuna onse.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 34:25
10 Mawu Ofanana  

Ndipo anapha Hamori ndi Sekemu mwana wake ndi lupanga, natulutsa Dina m'nyumba ya Sekemu nachoka naye.


Koma Hezekiya sanabwezere monga mwa chokoma anamchitira, pakuti mtima wake unakwezeka; chifukwa chake unamdzera mkwiyo iye, ndi Yuda, ndi Yerusalemu.


Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona; ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.


Ndipo tsono iphani amuna onse mwa anawo, iphaninso akazi onse akudziwa mwamuna mogona naye.


Ndipo anawathira nkhondo Amidiyani, monga Yehova adamuuza Mose; nawapha amuna onse.


Pakuti ana a Israele anayenda m'chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.


Ndipo kunali, atatha kudula mtundu wonse, anakhala m'malo mwao m'chigono mpaka adachira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa