Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 33:13 - Buku Lopatulika

13 Ndipo anati kwa iye, Mbuyanga adziwa kuti ana ali anthete, ndipo nkhosa ndi zoweta ndili nazo zilinkuyamwitsa: ndipo akathamangitsa tsiku limodzi zoweta zonse zidzafa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Ndipo anati kwa iye, Mbuyanga adziwa kuti ana ali ambowa, ndipo nkhosa ndi zoweta ndili nazo zilinkuyamwitsa: ndipo akathamangitsa tsiku limodzi zoweta zonse zidzafa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Tsono Yakobe adati, “Mbuyanga, mukudziŵa kuti anaŵa atopa, ndipo ndiyenera kusamalanso nkhosa ndi ng'ombe zimene zili ndi tiana. Ndikazikusa mofulumira kwambiri, ngakhale tsiku limodzi lokha, zifa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 33:13
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Esau anati, Tiyeni timuke; nditsogolera ndine.


Mbuyanga atsogoleretu kapolo wake, ndipo ine ndidzazitsogolera pang'onopang'ono monga mwa mayendedwe a zoweta zili pamaso panga, ndi monga mwa mayendedwe a ana, mpaka ndifike kwa mbuyanga ku Seiri.


Ndipo Davide anati, Solomoni mwana wanga ndiye mnyamata ndi wosakhwima, ndi nyumba imene adzaimangira Yehova ikhale yaikulu yopambana, yomveka ndi ya ulemerero mwa maiko onse; ndiikonzeretu mirimo. Momwemo Davide anakonzeratu mochuluka asanamwalire.


Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa, awete Yakobo, anthu ake, ndi Israele, cholowa chake.


Wolungama asamalira moyo wa choweta chake; koma chifundo cha oipa ndi nkhanza.


Iye adzadyetsa zoweta zake ngati mbusa, nadzasonkhanitsa anaankhosa m'manja mwake, nadzawatengera pa chifuwa chake, ndipo adzatsogolera bwinobwino zimene ziyamwitsa.


Ndipo anthuwo anatero; natenga ng'ombe ziwiri zamkaka, nazimanga pagaleta, natsekera anao kwao;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa