Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 25:5 - Buku Lopatulika

5 Ndipo Abrahamu anampatsa Isaki zonse anali nazo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Ndipo Abrahamu anampatsa Isaki zonse anali nazo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Abrahamu adasiyira Isaki zonse zimene anali nazo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 25:5
18 Mawu Ofanana  

Yehova wamdalitsa mbuyanga kwambiri; ndipo analemera kwakulukulu; ndipo anampatsa iye nkhosa ndi ng'ombe, ndi siliva ndi golide, ndi akapolo ndi adzakazi, ndi ngamira ndi abulu.


Ndipo Sara mkazi wake wa mbuyanga anambalira mbuyanga mwana wamwamuna, mkaziyo anali wokalamba; ndipo anampatsa mwanayo zonse ali nazo.


Ana a Midiyani: Efa, ndi Efere, ndi Hanoki, ndi Abida, ndi Elida. Onse amenewa ndi ana a Ketura.


ndipo anali ndi chuma cha nkhosa, ndi chuma cha zoweta, ndi banja lalikulu: ndipo Afilisti anamchitira iye nsanje.


Munakwera kunka kumwamba, munapita nao undende kuuyesa ndende; munalandira zaufulu mwa anthu, ngakhale mwa opikisana nanu, kuti Yehova Mulungu akakhale nao.


Zinthu zonse zinaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu adziwa Mwana, koma Atate yekha, ndi palibe wina adziwa Atate, koma Mwana yekha, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira.


Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi padziko lapansi.


monga mwampatsa Iye ulamuliro pa thupi lililonse, kuti onse amene mwampatsa Iye, awapatse iwo moyo wosatha.


Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lake.


ndipo ngati ana, pomweponso olowa nyumba; inde olowa nyumba ake a Mulungu, ndi olowa anzake a Khristu; ngatitu ife timva zowawa pamodzi naye, kuti tikalandirenso ulemerero pamodzi ndi Iye.


Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?


Koma ngati muli a Khristu, muli mbeu ya Abrahamu, nyumba monga mwa lonjezano.


Koma ife, abale, monga Isaki, tili ana a lonjezano.


Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,


koma pakutha pake pa masiku ano analankhula ndi ife ndi Mwana amene anamuika wolowa nyumba wa zonse, mwa Iyenso analenga maiko ndi am'mwamba omwe;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa