Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 24:44 - Buku Lopatulika

44 ndipo iye akati kwa ine, Imwatu iwe, ndiponso ndidzatungira ngamira zako; yemweyo akhale mkazi amene Yehova wamsankhira mwana wa mbuyanga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

44 ndipo iye akati kwa ine, Imwatu iwe, ndiponso ndidzatungira ngamira zako; yemweyo akhale mkazi amene Yehova wamsankhira mwana wa mbuyanga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

44 Iye akandiyankha kuti: Imwani ndipo ndimwetsanso ngamira zanuzi, ameneyo ndiye akhale namwali amene Chauta wamsankha kuti akhale mkazi wa mwana wa mbuyanga.’

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

44 ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”

Onani mutuwo Koperani




Genesis 24:44
11 Mawu Ofanana  

Ndipo nthitiyo anaichotsa Yehova Mulungu mwa Adamu anaipanga mkazi, ndipo ananka naye kwa Adamu.


ndipo pakhale kuti namwali amene ndidzati kwa iye, Tulatu mtsuko wako, ndimwe; ndipo iye adzati, Imwa, ndipo ndidzamwetsanso ngamira zako; yemweyo akhale mkazi wosankhira mnyamata wanu Isaki; ndipo chotero ndidzadziwa kuti mwamchitira mbuyanga ufulu.


taonani, ine ndiima pa kasupe wa madzi, ndipo pakhale, kuti namwali amene atuluka kudzatunga madzi ndimwe pang'ono m'mtsuko mwako;


Ndisanathe kunena m'mtima mwanga, taonani, Rebeka anatuluka ndi mtsuko wake pa phewa lake, natsikira ku kasupe, natunga: ndipo ndinati kwa iye, Ndimwetu.


Maere aponyedwa pamfunga; koma ndiye Yehova alongosola zonse.


Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino; Yehova amkomera mtima.


Nyumba ndi chuma ndizo cholowa cha atate; koma mkazi wanzeru achokera kwa Yehova.


Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.


komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.


Musaiwale kuchereza alendo; pakuti mwa ichi ena anachereza angelo osachidziwa.


Chotsalira, khalani nonse a mtima umodzi, ochitirana chifundo, okondana ndi abale, achisoni, odzichepetsa;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa