Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 24:26 - Buku Lopatulika

26 Munthuyo ndipo anawerama mutu namyamika Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

26 Munthuyo ndipo anawerama mutu namyamika Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

26 Pamenepo munthu uja adaŵerama nkupembedza Chauta,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

26 Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,

Onani mutuwo Koperani




Genesis 24:26
19 Mawu Ofanana  

Ndipo Abrahamu anati kwa anyamata ake, Khalani kuno ndi bulu, ine ndi mwanayu tinka uko, ndipo tikapemphera ndi kubweranso kwa inu.


Natinso kwa iye, Tili nao udzu ndi zakudya zambiri ndi malo ogona.


Ndipo ndinawerama mutu wanga ndi kulambira Yehova, ndi kumyamikira Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, amene ananditsogolera ine m'njira yakuona, kuti ndikamtengere mwana wamwamuna wake mwana wa mkazi wa mphwake wa mbuyanga.


Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi.


Ndipo Davide anati kwa khamu lonse, Mulemekeze tsono Yehova Mulungu wanu. Ndi khamu lonse linalemekeza Yehova Mulungu wa makolo ao, nawerama, nalambira Yehova, ndi mfumu.


Ndipo Yehosafati anawerama mutu wake, nkhope yake pansi; ndi Ayuda onse, ndi okhala mu Yerusalemu anagwa pansi pamaso pa Yehova, nalambira Yehova.


Hezekiya mfumu ndi akalonga nauzanso Alevi aimbire Yehova zomlemekeza ndi mau a Davide ndi a Asafu mlauli. Ndipo anaimbira zomlemekeza mokondwera, nawerama mitu yao, nalambira.


Pamenepo Ezara analemekeza Yehova Mulungu wamkulu. Navomereza anthu onse, ndi kuti, Amen, Amen; nakweza manja ao, nawerama, nalambira Yehova nkhope zao pansi.


Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira; onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake, ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.


Dziko lonse lapansi lidzakugwadirani, ndipo lidzakuimbirani; ndzaimbira dzina lanu.


Okhala m'chipululu adzagwadira pamaso pake; ndi adani ake adzaluma nthaka.


Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.


Mudzati, Ndiko nsembe ya Paska wa Yehova, amene anapitirira nyumba za ana a Israele mu Ejipito, pamene anakantha Aejipito, napulumutsa nyumba zathu.


Ndipo Mose anafulumira, naweramira pansi nalambira.


Ndipo anthuwo anakhulupirira; ndipo pamene anamva kuti Yehova adawazonda ana a Israele, ndi kuti adaona mazunzo ao, anawerama, nalambira Mulungu.


Ndidzafika kwa Yehova ndi chinai, ndi kuwerama kwa Mulungu Wam'mwamba? Kodi ndifike kwa Iye ndi nsembe zopsereza, ndi anaang'ombe a chaka chimodzi?


kuti m'dzina la Yesu bondo lililonse lipinde, la za m'mwamba ndi za padziko, ndi za pansi padziko,


Ndipo kunali, pakumva Gideoni kufotokozera kwa lotolo ndi tanthauzo lake, anadziwerama; nabwera ku misasa ya Israele nati, Taukani, pakuti Yehova wapereka a m'misasa a Midiyani m'dzanja lanu.


chifukwa chake inenso ndinampereka kwa Yehova; masiku onse a moyo wake aperekedwa kwa Yehova. Ndipo analambira Yehova pomwepo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa