Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 22:20 - Buku Lopatulika

20 Ndipo panali zitapita izi, anauza Abrahamu kuti, Taonani, Milika iyenso anambalira Nahori mphwako ana;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Ndipo panali zitapita izi, anauza Abrahamu kuti, Taonani, Milika iyenso anambalira Nahori mphwako ana;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Pambuyo pake Abrahamu adamva kuti Milika adabalira Nahori mbale wake ana asanu ndi atatu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 22:20
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Tera anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi awiri, nabala Abramu, ndi Nahori ndi Harani.


Mibadwo ya Tera ndi iyi: Tera anabala Abramu, ndi Nahori, ndi Harani; ndipo Harani anabala Loti.


Ndipo Abramu ndi Nahori, anadzitengera okha akazi; dzina lake la mkazi wa Abramu ndilo Sarai; ndi dzina lake la mkazi wa Nahori ndilo Milika, mwana wake wa Harani, atate wake wa Milika, ndi atate wake wa Isika.


Zitapita izo, mau a Yehova anadza kwa Abramu m'masomphenya, kuti, Usaope, Abramu, Ine ndine chikopa chako ndi mphotho yako yaikulukulu.


Uzi woyamba ndi Buzi mphwake, ndi Kemuwele atate wake wa Aramu;


Ndipo mnyamatayo anatenga ngamira khumi za mbuyake, namuka: chifukwa kuti chuma chonse cha mbuyake chinali m'dzanja lake: ndipo anachoka namuka ku Mesopotamiya, kumzinda wa Nahori.


Ndipo panali, asanathe kunena, taonani, anatuluka Rebeka, amene anambala Betuele, mwana wamwamuna wa Milika, mkazi wa Nahori mphwake wa Abrahamu, ndi mtsuko wake paphewa pake.


Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Ine ndine mwana wa Betuele mwana wamwamuna wa Milika, amene anambalira Nahori.


Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori, Mulungu wa atate wao aweruze pa ife. Ndipo Yakobo analumbirira pa Kuopsa kwa atate wake Isaki.


Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa, momwemo mau abwino akuchokera kudziko lakutali.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa