Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 16:8 - Buku Lopatulika

8 Ndipo anati, Hagara, mdzakazi wake wa Sarai, ufumira kuti? Unka kuti? Ndipo anati, Ndithawa ine kumaso kwake kwa wakuka wanga Sarai.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Ndipo anati, Hagara, mdzakazi wake wa Sarai, ufumira kuti? Unka kuti? Ndipo anati, Ndithawa ine kumaso kwake kwa wakuka wanga Sarai.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Ndipo adati, “Iwe Hagara, mdzakazi wa Sarai, kodi ukuchokera kuti, nanga ukupita kuti?” Iye adayankha kuti “Ndikuthaŵa mbuyanga Sarai.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”

Onani mutuwo Koperani




Genesis 16:8
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Sarai mkazi wake wa Abramu sanambalire iye mwana; ndipo anali ndi mdzakazi, wa ku Ejipito, dzina lake Hagara.


Ndipo analowa kwa Hagara, ndipo iye anatenga pakati. Pamene anaona kuti anatenga pakati, anapeputsa wakuka wake m'maso mwake.


Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Bwera kwa wakuka wako, udzichepetse wekha pamanja pake.


Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? Usaope; chifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.


Ndipo Yehova Mulungu anaitana mwamunayo nati kwa iye, Uli kuti?


Ndipo anati, Wachita chiyani? Mau a mwazi wa mphwako andifuulira Ine kunthaka.


Ndipo atamva Eliya, anafunda nkhope yake ndi chofunda chake, natuluka, naima pa khomo la phangalo. Ndipo taonani, anamdzera mau akunena naye, Uchitanji kuno, Eliya?


Nafika kuphanga, nagona kumeneko, ndipo taonani, mau a Yehova anamfikira, nati kwa iye, Uchitanji pano, Eliya?


Pamenepo analowa, naima kwa mbuye wake. Ndipo Elisa ananena naye, Ufuma kuti Gehazi? Nati, Ngati mnyamata wanu wayenda konse?


Ngati mkulu akukwiyira, usasiye malo ako; chifukwa chifatso chipembedza utachimwa kwambiri.


Pamene anakweza maso ake anaona munthu wa pa ulendoyo m'khwalala la mzinda; ndi nkhalambayo inati, Umuka kuti? Ufumira kuti?


Chifukwa chake mbuye wanga mfumu amvere mau a kapolo wake. Ngati ndi Yehova anakuutsirani inu kutsutsana ndi ine, alandire chopereka; koma ngati ndi ana a anthu, atembereredwe pamaso pa Yehova, pakuti anandipirikitsa lero kuti ndisalandireko cholowa cha Yehova, ndi kuti, Muka, utumikire milungu ina.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa