Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 1:6 - Buku Lopatulika

6 Ndipo anati Mulungu, Pakhale thambo pakati pamadzi, lilekanitse madzi ndi madzi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndipo anati Mulungu, Pakhale thambo pakati pamadzi, lilekanitse madzi ndi madzi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Kenaka Mulungu adati, “Pakhale cholekanitsa madzi, kuti madziwo akhale pa malo aŵiri olekana,” ndipo zidachitikadi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”

Onani mutuwo Koperani




Genesis 1:6
23 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anati, Pakhale zounikira pathambo la kumwamba, zakulekanitsa usana ndi usiku; zikhale zizindikiro ndi nyengo, ndi masiku, ndi zaka;


Ndipo anati Mulungu, Madzi abale zochuluka zamoyo zoyendayenda, ndi mbalame ziuluke pamwamba padziko lapansi ndi pamlengalenga.


Mwa mzimu wake anyezimiritsa thambo; dzanja lake linapyoza njoka yothawayo.


Asenzetsanso mtambo wakuda bii madzi, afunyulula mtambo wokhalamo mphezi yake;


Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye, ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?


muvala ulemu ndi chifumu. Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi chovala; ndi kuyala thambo ngati nsalu yotchinga.


Mlemekezeni, m'mwambamwamba, ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.


Aleluya. Lemekezani Mulungu m'malo ake oyera; mlemekezeni m'thambo la mphamvu yake.


Zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu; ndipo thambo lionetsa ntchito ya manja ake.


Usana ndi usana uchulukitsa mau, ndipo usiku ndi usiku uonetsa nzeru.


Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova; ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwake khamu lao lonse.


Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa; analamulira, ndipo chinakhazikika.


Mitambo ikadzala mvula, itsanulira pansi; mtengo ukagwa kumwera pena kumpoto, pomwe unagwa mtengowo udzakhala pomwepo.


Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekezero a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati chinsalu, naliyala monga hema wakukhalamo;


Koma Yehova ndiye Mulungu woona; ndiye Mulungu wamoyo, mfumu yamuyaya; pa mkwiyo wake dziko lapansi lidzanthunthumira, ndi amitundu sangapirire ukali wake.


Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, wakhazika dziko lapansi ndi nzeru yake, ndi luso anayala thambo;


Katundu wa mau a Yehova wakunena Israele. Atero Yehova, wakuyala miyamba, ndi kuika maziko a dziko lapansi, ndi kulenga mzimu wa munthu m'kati mwake;


Pakuti ichi aiwala dala, kuti miyamba inakhala kale lomwe, ndi dziko lidaungika ndi madzi ndi mwa madzi, pa mau a Mulungu;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa