Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 36:10 - Buku Lopatulika

10 Ndipo analumikiza nsalu zisanu ina ndi inzake; nalumikiza nsalu zisanu zina ina ndi inzake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndipo analumikiza nsalu zisanu ina ndi inzake; nalumikiza nsalu zisanu zina ina ndi inzake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Ndipo adasokerera nsalu zisanu, kuti zikhale chinsalu chimodzi, zisanu zinazonso adazisokerera nkukhalanso chinsalu chimodzi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 36:10
15 Mawu Ofanana  

Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda woundana bwino:


Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu kuti abale akhale pamodzi!


Nsalu zisanu zilumikizane ina ndi inzake; ndi nsalu zisanu zina zilumikizane ina ndi inzake.


Ndipo anaika magango ansalu yamadzi m'mphepete mwake mwa nsalu imodzi ku mkawo wa chilumikizano; nachita momwemo m'mphepete mwake mwa nsalu ya kuthungo, ya chilumikizano chachiwiri.


Utali wake wa nsalu yophimba imodzi ndiwo mikono makumi awiri kudza isanu ndi itatu, ndi kupingasa kwake kwa nsalu imodzi mikono inai; nsalu zonse zinafanana muyeso wao.


Pakuti pamenepo ndidzapatsa mitundu ya anthu mlomo woyera, kuti onsewa aitanire pa dzina la Yehova kumtumikira ndi mtima umodzi.


Ndipo pakufika tsiku la Pentekoste, anali onse pamodzi pamalo amodzi.


Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti munene chimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'chiweruziro chomwecho.


Koma tsopano pali ziwalo zambiri, koma thupi limodzi.


Koma inu ndinu thupi la Khristu, ndi ziwalo, yense pa yekha.


amene ali thupi lake, mdzazidwe wa Iye amene adzaza zonse m'zonse.


kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;


Tonsefe amene tsono tidakonzeka amphumphu, tilingirire ichi mumtima; ndipo ngati kuli kanthu mulingirira nako kwina mumtima, akanso Mulungu adzavumbulutsira inu;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa