Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 17:15 - Buku Lopatulika

15 Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalitcha dzina lake Yehova Nisi:

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 Ndipo Mose adamanga guwa nalitcha kuti, “Chauta ndiye mbendera yanga.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 17:15
9 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anaonekera kwa Abramu nati, Ndidzapatsa mbeu yako dziko lino: pamenepo anammangira Yehova guwa la nsembe amene anamuonekera iye.


Ndipo iye anachoka kumeneko kunka kuphiri la kum'mawa kwa Betele, namanga hema wake; Betele anali kumadzulo, ndi Ai anali kum'mawa: kumeneko ndipo anammangira Yehova guwa la nsembe, naitanira dzina la Yehova.


Ndipo Abrahamu anatcha dzina lake la malowo Yehova-Yire: monga ati lero lomwe, M'phiri la Yehova chidzaoneka.


Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, natcha pamenepo El-Elohe-Israele.


Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu, aikweze chifukwa cha choonadi.


Ndipo Mose analembera mau onse a Yehova, nalawira kuuka mamawa, namanga guwa la nsembe patsinde paphiri, ndi zoimiritsa khumi ndi ziwiri, kwa mafuko khumi ndi awiri a Israele.


Ndipo upange guwa la nsembe la mtengo wakasiya, utali wake mikono isanu, ndi kupingasa kwake mikono isanu, guwa la nsembelo likhale laphwamphwa, ndi msinkhu wake mikono itatu.


Pakuchiona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pake; ndipo Aroni anafuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova.


Pamenepo Gideoni anammangira Yehova guwa la nsembe pomwepo; nalitcha Yehova-ndiye-mtendere; likali mu Ofura wa Aabiyezere ndi pano pomwe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa