Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 15:24 - Buku Lopatulika

24 Ndipo anthu anadandaulira Mose, ndi kuti, Tidzamwa chiyani?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

24 Ndipo anthu anadandaulira Mose, ndi kuti, Tidzamwa chiyani?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

24 Apo anthu aja adadandaulira Mose, namufunsa kuti, “Kodi ife timwa chiyani?”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

24 Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 15:24
19 Mawu Ofanana  

Koma anaiwala ntchito zake msanga; sanalindire uphungu wake:


Ndipo anati kwa Mose, Kodi mwatichotsera kuti tikafe m'chipululu chifukwa panalibe manda mu Ejipito? Nchiyani ichi mwatichitira kuti mwatitulutsa mu Ejipito?


Ndipo khamu lonse la ana a Israele linadandaulira Mose ndi Aroni m'chipululu;


ndipo ananena nao, Yehova akupenyeni, naweruze; pakuti mwatinyansitsa pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ake, ndi kuwapatsa lupanga m'dzanja lao kutipha nalo.


popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikiro zanga, ndidazichita mu Ejipito ndi m'chipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;


Chifukwa chake, iwe ndi khamu lonse mwasonkhana kutsutsana ndi Yehova; ndipo Aroniyo ndani, kuti mudandaule pa iye?


Koma m'mawa mwake khamu lonse la ana a Israele anadandaula pa Mose ndi Aroni, nati, Mwapha anthu a Yehova, inu.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kuiika chakuno cha mboni, isungike ikhale chizindikiro cha pa ana opikisana; kuti unditsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.


Ndipo anthu ananena motsutsana ndi Mulungu, ndi Mose, ndi kuti, Mwatikwezeranji kutichotsa ku Ejipito kuti tifere m'chipululu? Pakuti mkate ndi madzi palibe, ndi mtima wathu walema nao mkate wachabe uwu.


Chifukwa chake ndinena kwa inu, Musadere nkhawa moyo wanu, chimene mudzadya ndi chimene mudzamwa; kapena thupi lanu, chimene mudzavala. Kodi moyo suli woposa chakudya, ndi thupi loposa chovala?


Kapena musadandaula, monga ena a iwo anadandaula, naonongeka ndi woonongayo.


Chitani zonse kopanda madandaulo ndi makani,


Amenewo ndiwo odandaula, oderera, akuyenda monga mwa zilakolako zao (ndipo pakamwa pao alankhula zazikuluzikulu), akutama anthu chifukwa cha kupindula nako.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa