Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Akolose 3:20 - Buku Lopatulika

20 Ana inu, mverani akubala inu m'zonse, pakuti ichi Ambuye akondwera nacho.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Ana inu, mverani akubala inu m'zonse, pakuti ichi Ambuye akondwera nacho.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Inu ana, muzimvera anakubala anu pa zonse, pakuti kutero kumakondwetsa Ambuye.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.

Onani mutuwo Koperani




Akolose 3:20
23 Mawu Ofanana  

ndiponso kuti Yakobo anamvera atate wake ndi amake, nanka ku Padanaramu;


Uzilemekeza atate wako ndi amai ako; kuti achuluke masiku ako m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.


Wotemberera atate wake ndi amake, nyali yake idzazima mu mdima woti bii.


Pali mbadwo wotemberera atate ao, osadalitsa amai ao.


Diso lochitira atate wake chiphwete, ndi kunyoza kumvera amake, makwangwala a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya.


Mwananga, sunga malangizo a atate wako, usasiye malamulo a mai ako;


Ndipo ife tamva mau a Yonadabu mwana wa Rekabu kholo lathu m'zonse zimene anatiuza ife, zakuti tisamwe vinyo masiku athu onse, ife, akazi athu, ana athu aamuna ndi aakazi;


Mwa iwe anapepula atate ndi mai, pakati pa iwe anamchitira mlendo momzunza, mwa iwe anazunza ana amasiye, ndi mkazi wamasiye.


Aliyense aope mai wake, ndi atate wake; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.


Mwana alemekeza atate wake, ndi mnyamata mbuye wake; ngati Ine tsono ndine atate, uli kuti ulemu wanga? Ngati Ine ndine mbuye, kundiopa kuli kuti? Ati Yehova wa makamu kwa inu ansembe akupeputsa dzina langa. Ndipo mukuti, Tapeputsa dzina lanu motani?


Lemekeza atate wako ndi amai ako, ndipo, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.


Komatu monga Mpingo amvera Khristu, koteronso akazi amvere amuna ao m'zinthu zonse.


Wotembereredwa iye wakupeputsa atate wake kapena mai wake. Ndi anthu onse anene, Amen.


Lemekeza atate wako ndi amai ako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako achuluke, ndi kuti chikukomere, m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.


Koma ndili nazo zonse, ndipo ndisefukira; ndadzazidwa, popeza ndalandira kwa Epafrodito zija zidachokera kwanu, mnunkho wa fungo labwino, nsembe yolandirika, yokondweretsa Mulungu.


kuti mukayenda koyenera Ambuye kukamkondweretsa monsemo, ndi kubala zipatso mu ntchito yonse yabwino, ndi kukula m'chizindikiritso cha Mulungu;


Akapolo inu, mverani m'zonse iwo amene ali ambuye monga mwa thupi, wosati ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu ndi mtima wakulinga kumodzi, akuopa Ambuye;


Akapolo amvere ambuye ao a iwo okha, nawakondweretse m'zonse; osakana mau ao;


akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.


Ndipo ananena naye, Zonse muzinena ndidzachita.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa