Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Ahebri 4:1 - Buku Lopatulika

1 Chifukwa chake tiope kuti kapena likatsala lonjezano lakulowa mpumulo wake, wina wa inu angaoneke ngati adaliperewera.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Chifukwa chake tiope kuti kapena likatsala lonjezano lakulowa mpumulo wake, wina wa inu angaoneke ngati adaliperewera.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Lonjezo la Mulungu lakuti tidzaloŵa mu mpumulo umene Iye adatikonzera, lilipobe. Tsono tichenjere kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wopezeka kuti walephera kuloŵamo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Popeza lonjezo lakuti tidzalowe mu mpumulo umene anatilonjeza lilipobe, tiyeni tisamale kuti pasakhale wina aliyense mwa inu wodzalephera kulowamo.

Onani mutuwo Koperani




Ahebri 4:1
28 Mawu Ofanana  

Wanzeru amaopa nasiya zoipa; koma wopusa amanyada osatekeseka.


Wodala munthu wakuopa kosalekeza; koma woumitsa mtima wake adzagwa m'zoipa.


ndipo ndidzapangana nao pangano lamuyaya, kuti sindidzawachokera kuleka kuwachitira zabwino; koma ndidzalonga kuopsa kwanga m'mitima yao, kuti asandichokere.


Monga mwa kuwerenga kwa masiku amene munazonda dziko, masiku makumi anai, tsiku limodzi kuwerenga chaka chimodzi, mudzasenza mphulupulu zanu, zaka makumi anai, ndipo mudzadziwa kuti ndaleka lonjezano langa.


Koma kapolo woipa akanena mumtima mwake, Mbuye wanga wachedwa;


Chifukwa chake lapani, bwererani kuti afafanizidwe machimo anu, kotero kuti zidze nyengo zakutsitsimutsa zochokera kunkhope ya Ambuye;


Chabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi chikhulupiriro chako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:


pakuti onse anachimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu;


Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.


Ndipo ochita naye pamodzi tidandauliranso kuti musalandire chisomo cha Mulungu kwachabe inu,


Mulibe kanthu ndi Khristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana nacho chisomo.


ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sangathe kudzikana yekha.


ndi kuyang'anira kuti pangakhale wina wakuperewera chisomo cha Mulungu, kuti ungapuke muzu wina wa kuwawa mtima ungavute inu, ndipo aunyinji angadetsedwe nao;


Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuke, pomkana Iye amene anawachenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa Iye wa Kumwamba;


Kumbukirani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira chitsiriziro cha mayendedwe ao mutsanze chikhulupiriro chao.


Monga ndinalumbira mu ukali wanga: Ngati adzalowa mpumulo wanga!


Chifukwa chake tichite changu cha kulowa mpumulowo, kuti wina angagwe m'chitsanzo chomwe cha kusamvera.


Momwemo utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu.


Chifukwa chake Yehova Mulungu wa Israele akuti, Ndinaterodi kuti banja lako ndi banja la kholo lako lidzayenda pamaso panga nthawi zonse; koma tsopano Yehova ati, Chikhale kutali ndi Ine; popeza amene andilemekeza Ine, Inenso ndidzawalemekeza iwowa, ndipo akundipeputsa Ine, adzapeputsidwa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa