Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Ahebri 3:9 - Buku Lopatulika

9 chimene makolo anu anandiyesa nacho, ndi kundivomereza, naona ntchito zanga zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 chimene makolo anu anandiyesa nacho, ndi kundivomereza, naona ntchito zanga zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Mulungu akuti, Pamene paja, makolo anu adaandiputa pakundiyesa, ndipo adaona zimene ndidaŵachita pa zaka makumi anai.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa, ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.

Onani mutuwo Koperani




Ahebri 3:9
17 Mawu Ofanana  

Pamene makolo anu anandisuntha, anandiyesa, anapenyanso chochita Ine.


Inu munaona chimene ndinachitira Aejipito; ndi kuti ndanyamula inu monga pa mapiko a mphungu, ndi kubwera nanu kwa Ine ndekha.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uzitero ndi ana a Israele, kuti, Mwapenya nokha kuti ndalankhula nanu, kuchokera kumwamba.


Ndipo ndinakukwezani kuchokera m'dziko la Ejipito, ndi kukutsogolerani zaka makumi anai m'chipululu, kuti mulandire dziko la Aamori likhale cholowa chanu.


Ndipo ana anu adzakhala oyendayenda m'chipululu zaka makumi anai, nadzasenza kupulukira kwanu, kufikira mitembo yanu yatha m'chipululu.


Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Mukani, muuze Yohane zimene mwaziona, nimwazimva; anthu akhungu alandira kuona kwao, opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ogontha akumva, akufa aukitsidwa, kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.


Koma Elimasi watsengayo (pakuti dzina lake litero posandulika) anawakaniza, nayesa kupatutsa kazembe asakhulupirire.


Ameneyo anawatsogolera, natuluka nao atachita zozizwa ndi zizindikiro mu Ejipito, ndi mu Nyanja Yofiira, ndi m'chipululu zaka makumi anai.


Koma maso anu anapenya ntchito yonse yaikulu ya Yehova anaichita.


Ndipo Mose anaitana Israele wonse, nati nao, Munapenya inu zonse zimene Yehova anachitira Farao, ndi anyamata ake onse, ndi dziko lake lonse, pamaso panu m'dziko la Ejipito;


Maso anu anapenya chochita Yehova chifukwa cha Baala-Peori; pakuti amuna onse amene anatsata Baala-Peori, Yehova Mulungu wanu anawaononga pakati panu.


Chokhachi, dzichenjerani nokha, ndi kusunga moyo wanu mwachangu, kuti mungaiwale zinthuzi adaziona maso anu, ndi kuti zisachoke kumtima kwanu masiku onse a moyo wanu; koma muzidziwitsa ana anu ndi zidzukulu zanu.


Ndipo mukumbukire njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakuyendetsani m'chipululu zaka izi makumi anai, kuti akuchepetseni, kukuyesani, kudziwa chokhala mumtima mwanu, ngati mudzasunga malamulo ake, kapena iai.


Zovala zanu sizinathe pathupi panu, phazi lanu silinatupe zaka izi makumi anai.


ndipo munapenya zonse Yehova Mulungu anachitira mitundu iyi yonse ya anthu chifukwa cha inu; pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anakuthirirani nkhondo.


Ndipo pamene anafuula kwa Yehova, anaika mdima pakati pa inu ndi Aejipito nawatengera nyanja, nawamiza; ndi maso anu anapenya chochita Ine mu Ejipito; ndipo munakhala m'chipululu masiku ambiri.


Pakuti ana a Israele anayenda m'chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa