Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Aefeso 5:21 - Buku Lopatulika

21 ndi kumverana wina ndi mnzake m'kuopa Khristu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 ndi kumverana wina ndi mnzake m'kuopa Khristu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Inu amene mumaopa Khristu, muzimverana.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.

Onani mutuwo Koperani




Aefeso 5:21
20 Mawu Ofanana  

Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Bwera kwa wakuka wako, udzichepetse wekha pamanja pake.


Ndi akulu onse, ndi amuna amphamvu onse, ndi ana aamuna onse omwe a mfumu Davide, anagonjeratu kwa Solomoni mfumu.


Ndipo tsono, kuopa Yehova kukhale pa inu, musamalire ndi kuchita; pakuti palibe chosalungama kwa Yehova Mulungu wathu, kapena kusamalira monga mwa nkhope ya munthu, kapena kulandira mphatso.


Koma akazembe akale ndisanakhale ine, analemetsa anthu, nadzitengera kwa iwo mkate, ndi vinyo, pamodzi ndi siliva masekeli makumi anai; angakhale anyamata ao anachita ufumu pa anthu; koma sindinatero ine, chifukwa cha kuopa Mulungu.


Ndinatinso, Chinthu muchitachi si chokoma ai; simuyenera kodi kuyenda m'kuopa Mulungu wathu, chifukwa cha mnyozo wa amitundu, ndiwo adani athu?


Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe, osadudukira anthu osinthasintha.


kuti inunso muvomere otere, ndi yense wakuchita nao, ndi kugwiritsa ntchito.


Podziwa tsono kuopsa kwa Ambuye, tikopa anthu, koma tionetsedwa kwa Mulungu; ndipo ndiyembekezanso kuti tionetsedwa m'zikumbu mtima zanu.


Pokhala nao tsono malonjezano amenewa, okondedwa, tidzikonzere tokha kuleka chodetsa chonse cha thupi ndi cha mzimu, ndi kutsiriza chiyero m'kuopa Mulungu.


Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.


Akazi inu, mverani amuna anu a inu eni, monga kumvera Ambuye.


Komatu monga Mpingo amvera Khristu, koteronso akazi amvere amuna ao m'zinthu zonse.


musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;


Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse.


woweruza bwino nyumba yake ya iye yekha, wakukhala nao ana ake omvera iye ndi kulemekezeka konse.


Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akachite ndi chimwemwe, osati mwachisoni: pakuti ichi sichikupindulitsani inu.


Tadzigonjani kwa zoikika zonse za anthu, chifukwa cha Ambuye; ngakhale kwa mfumu, monga mutu wa onse;


Chitirani ulemu anthu onse. Kondani abale. Opani Mulungu, Chitirani mfumu ulemu.


Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu. Koma nonsenu muvale kudzichepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo kwa odzichepetsa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa