Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 21:6 - Buku Lopatulika

6 Mutipatse ana ake aamuna asanu ndi awiri, ndipo tidzawapachika kwa Yehova mu Gibea wa Saulo, wosankhika wa Yehova. Mfumu niti, Ndidzawapereka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Mutipatse ana ake amuna asanu ndi awiri, ndipo tidzawapachika kwa Yehova m'Gibea wa Saulo, wosankhika wa Yehova. Mfumu niti, Ndidzawapereka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Tsono mwa zidzukulu zake mutipatse anthu asanu ndi aŵiri, kuti ife tikaŵanyonge pamaso pa Chauta ku Gibiyoni, ku mzinda wa Saulo munthu wosankhidwa wa Chauta.” Apo mfumuyo idayankha kuti, “Chabwino, ndidzaŵapereka.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 21:6
22 Mawu Ofanana  

akali masiku atatu Farao adzakweza mutu wako ndi kuuchotsa, nadzakupachika iwe pamtengo: ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.


Koma anampachika wophika mkate wamkulu; monga Yosefe anawamasulira.


Ndipo Ahitofele, pakuona kuti sautsata uphungu wake anamanga bulu wake, nanyamuka, nanka kumzinda kwao, nakonza za pa banja lake, nadzipachika, nafa, naikidwa m'manda a atate wake.


Ndipo munthu wina anamuona, nauza Yowabu, nati, Onani, ndaona Abisalomu ali lende pathundu.


Pakuti nyumba yonse ya atate wanga inali anthu oyenera imfa pamaso pa mbuye wanga mfumu; koma inu munaika mnyamata wanu pakati pa iwo akudya pa gome lanu. Kuyenera kwanga nkutaninso kuti ndikaonjezere kudandaulira kwa mfumu?


Mkulu wao ndiye Ahiyezere, ndi Yowasi, ana a Semaa wa ku Gibea; ndi Yeziyele, ndi Peleti, ana a Azimaveti; ndi Beraka, ndi Yehu wa ku Anatoti,


Ndalamuliranso kuti aliyense adzasintha mau awa, usololedwe mtanda kunyumba kwake, namkweze, nampachike pomwepo; niyesedwa dzala nyumba yake chifukwa cha ichi;


ana aamuna khumi a Hamani mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande zofunkha.


Ndipo iye anataya pansi ndalamazo pa Kachisi, nachokapo, nadzipachika yekha pakhosi.


Ndipo kuyambira pamenepo anapempha mfumu; ndipo Mulungu anawapatsa Saulo mwana wa Kisi, munthu wa fuko la Benjamini, zaka makumi anai.


Munthu akakhala nalo tchimo loyenera imfa, kuti amuphe, ndipo wampachika;


Ndipo atatero, Yoswa anawakantha nawapha, nawapachika pa mitengo isanu; nalikupachikidwa pa mitengo mpaka madzulo.


Ndipo mfumu ya ku Ai, anampachika pamtengo mpaka madzulo; koma polowa dzuwa Yoswa analamulira kuti atsitse mtembo wake pamtengo; ndipo anauponya polowera pa chipata cha mzinda; naunjikako mulu waukulu wamiyala, mpaka lero lino.


Pamenepo Samuele anatenga nsupa ya mafuta, nawatsanulira pamutu pake, nampsompsona iye, nati, Sanakudzozeni ndi Yehova kodi, Mukhale mfumu ya pa cholowa chake?


Ndipo Samuele ananena ndi anthu onse, Mumuona kodi iye amene Yehova anamsankha, kuti palibe wina wakufanana naye pakati pa anthu onse? Ndipo anthu onse anafuula, kuti, Akhale ndi moyo mfumuyo.


Ndi Saulo yemwe anamuka kunyumba yake ku Gibea; ndipo am'khamu anatsagana naye iwo amene Mulungu adakhudza mitima yao.


Tsono mithengayo inafika ku Gibea kwa Saulo, nalankhula mau amenewa m'makutu a anthu; ndipo anthu onse anakweza mau, nalira misozi.


Chifukwa chake tsono undilumbirire ndi Yehova, kuti sudzatha mbeu yanga nditamuka ine, ndi kuti sudzaononga dzina langa m'nyumba ya atate wanga.


Ndipo Davide analumbirira Saulo. Saulo namuka kwao; koma Davide ndi anthu ake anakwera kunka kungaka.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa