Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 20:20 - Buku Lopatulika

20 Ndipo Yowabu anayankha nati, Iai ndi pang'ono ponse, chikhale kutali kwa ine, kuti ndingameze ndi kuononga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Ndipo Yowabu anayankha nati, Iai ndi pang'ono ponse, chikhale kutali kwa ine, kuti ndingameze ndi kuononga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Yowabu adayankha kuti, “Iyai, ine sindikufuna konse kuwononga mzinda uno.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 20:20
9 Mawu Ofanana  

Koma Amasa sanasamalire lupanga lili m'dzanja la Yowabu; chomwecho iye anamgwaza nalo m'mimba; nakhuthula matumbo ake pansi, osamgwazanso, nafa iye. Ndipo Yowabu ndi Abisai mbale wake analondola Sheba mwana wa Bikiri.


Ine ndine wa awo amene ali amtendere ndi okhulupirika mu Israele; inu mulikufuna kuononga mzinda ndi mai wa mu Israele; mudzamezeranji cholowa cha Yehova?


Mlanduwo suli wotere ai, koma munthu wa ku dziko lamapiri la Efuremu, dzina lake ndiye Sheba mwana wa Bikiri, anakweza dzanja lake pa mfumu Davide; mpereke iye yekha ndipo ndidzachoka mumzinda muno. Ndipo mkaziyo anati kwa Yowabu, Onani tidzakuponyerani mutu wake kutumphitsa linga.


Nati, Ndisachite ichi ndi pang'ono ponse, Yehova; ndimwe kodi mwazi wa anthu awa anapitawa ndi kutaya moyo wao? Chifukwa chake iye anakana kumwa. Izi anazichita ngwazi zitatuzi.


Taonani, zokoma zao sizili m'dzanja lao; (koma uphungu wa oipa unditalikira.)


Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino; koma uphungu wa oipa unditalikira.


Wobisa machimo ake sadzaona mwai; koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.


Mtima ndiwo wonyenga koposa, ndi wosachiritsika, ndani angathe kuudziwa?


Koma iye, pofuna kudziyesa yekha wolungama, anati kwa Yesu, Ndipo mnansi wanga ndani?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa