Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




2 Samueli 13:26 - Buku Lopatulika

26 Pomwepo Abisalomu anati, Ngati nkutero, mulole mbale wanga Aminoni apite nafe. Ndipo mfumu inanena naye, Iye apitirenji nawe?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

26 Pomwepo Abisalomu anati, Ngati nkutero, mulole mbale wanga Aminoni apite nafe. Ndipo mfumu inanena naye, Iye apitirenji nawe?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

26 Tsono Abisalomu adati, “Chabwino, ngati inu simupita, bwanji apite nao ndi mbale wanga Aminoniyu.” Apo mfumu idafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukufuna kuti iyeyu apite nao?”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”

Onani mutuwo Koperani




2 Samueli 13:26
8 Mawu Ofanana  

Ndipo mfumu inati kwa Abisalomu, Iai mwana wanga, tisapite tonse, kuti tingakuchulukire. Ndipo iye anaiumirira koma inakana kupita; koma inamdalitsa.


Koma Abisalomu anaiumirira iyo, nilola kuti Aminoni ndi ana aamuna onse a mfumu apite naye.


Ndipo Yowabu ananena ndi Amasa, Uli bwino mbale wanga? Ndipo Yowabu anagwira ndevu za Amasa ndi dzanja lake lamanja kuti ampsompsone.


Pofikanso Abinere ku Hebroni, Yowabu anampambutsa kupita naye pakati pa chipata kulankhula naye poduka mphepo; namgwaza pomwepo m'mimba, nafa, chifukwa cha mwazi wa Asahele mbale wake.


Pakamwa pake mposalala ngati mafuta amkaka, koma mumtima mwake munali nkhondo, mau ake ngofewa ngati mafuta oyenga, koma anali malupanga osololasolola.


Wakuda mnzake amanyenga ndi milomo yake; koma akundika chinyengo m'kati mwake.


Chifukwa chake atero Yehova wa makamu, Taonani, ndidzawasungunula, ndi kuwayesa, pakuti ndidzachitanji, chifukwa cha mwana wamkazi wa anthu anga?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa