Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Samueli 19:10 - Buku Lopatulika

10 Ndipo Saulo anayesa kupyoza Davide kumphatikiza kukhoma ndi mkondowo; koma iye anadzilanditsa kuchoka pamaso pa Saulo; ndipo analasa khoma; ndipo Davide anathawa napulumuka usiku uja.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndipo Saulo anayesa kupyoza Davide kumphatikiza kukhoma ndi mkondowo; koma iye anadzilanditsa kuchoka pamaso pa Saulo; ndipo analasa khoma; ndipo Davide anathawa napulumuka usiku uja.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Pomwepo Saulo adayesa kubaya Davide ndi kumkhomera ku chipupa. Koma Davide adauleŵa mkondowo, kotero kuti udangolasa chipupa. Ndipo adathaŵa napulumuka.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.

Onani mutuwo Koperani




1 Samueli 19:10
20 Mawu Ofanana  

Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi; msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.


Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu, ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.


Masautso a wolungama mtima achuluka, koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.


Woipa aunguza wolungama, nafuna kumupha.


pakuti mapazi ao athamangira zoipa, afulumira kukhetsa mwazi.


Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.


Palibe chida chosulidwira iwe chidzapindula; ndipo lilime lonse limene lidzakangana nawe m'chiweruzo udzalitsutsa. Ichi ndi cholowa cha atumiki a Yehova, ndi chilungamo chao chimene chifuma kwa Ine, ati Yehova.


Efuremu iwe, ndidzakuchitira chiyani? Yuda iwe, ndikuchitire chiyani? Pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam'mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa.


Koma pamene angakuzunzeni inu m'mudzi uwu, thawirani mwina: indetu ndinena kwa inu, Simudzaitha mizinda ya Israele, kufikira Mwana wa Munthu atadza.


Koma Iye anapyola pakati pao, nachokapo.


Anafunanso kumgwira Iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.


nazima mphamvu ya moto, napulumuka lupanga lakuthwa, analimbikitsidwa pokhala ofooka, anakula mphamvu kunkhondo, anapirikitsa magulu a nkhondo yachilendo.


Ndipo kunali m'mawa mwake, mzimu woipa wochokera kwa Mulungu unamgwira Saulo mwamphamvu, iye nalankhula moyaluka m'nyumba yake; koma Davide anaimba ndi dzanja lake, monga amachita tsiku ndi tsiku; koma m'dzanja la Saulo munali mkondo.


Ndipo Saulo anaponya mkondowo; pakuti anati, Ndidzapyoza Davide ndi kumphatikiza ndi khoma. Ndipo Davide analewa kawiri kuchoka pamaso pake.


Ndipo Saulo anamvera mau a Yonatani; nalumbira, Pali Yehova, sadzaphedwa iye.


Ndipo Saulo anamponyera mkondo kuti amgwaze; momwemo Yonatani anazindikira kuti atate wake anatsimikiza mtima kupha Davide.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa