Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




1 Akorinto 16:16 - Buku Lopatulika

16 kuti inunso muvomere otere, ndi yense wakuchita nao, ndi kugwiritsa ntchito.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 kuti inunso muvomere otere, ndi yense wakuchita nao, ndi kugwiritsa ntchito.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 Tsono ndikukupemphani kuti inunso muziŵamvera anthu otere, ndiponso aliyense wogwira ntchito ndi kutumikira modzipereka pamodzi nawo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka.

Onani mutuwo Koperani




1 Akorinto 16:16
20 Mawu Ofanana  

Pamenepo mzimu unavala Amasai, ndiye wamkulu wa makumi atatuwo, nati iye, Ndife anu, Davide, tivomerezana nanu mwana wa Yese inu: mtendere, mtendere ukhale ndi inu, ndi mtendere ukhale ndi athandizi anu; pakuti Mulungu wanu akuthandizani. Ndipo Davide anawalandira, nawaika akulu a magulu.


Kodi ntchito zake zonse munthu asauka nazo zimpindulira chiyani?


Moni kwa Trifena, ndi Trifosa amene agwiritsa ntchito mwa Ambuye. Moni kwa Perisi, wokondedwayo amene anagwiritsa ntchito zambiri mwa Ambuye.


Mupereke moni kwa Prisika ndi Akwila, antchito anzanga mwa Khristu Yesu,


Moni kwa Maria amene anadzilemetsa ndi ntchito zambiri zothandiza inu.


Moni kwa Urbano wantchito mnzathu mwa Khristu, ndi Stakisi wokondedwa wanga.


Ndipotu Mulungu anaika ena mu Mpingo, poyamba atumwi, achiwiri aneneri, achitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso za machiritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundumitundu.


Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; chilimo cha Mulungu, chimango cha Mulungu ndi inu.


ndi kumverana wina ndi mnzake m'kuopa Khristu.


Inde, ndikupemphaninso, mnzanga wa m'goli woona, muthandize akazi awa amene anakangalika nane pamodzi mu Uthenga Wabwino, pamodzi ndi Klemensinso, ndi otsala aja antchito anzanga, amene maina ao ali m'buku la Moyo.


ndi kukumbukira kosalekeza ntchito yanu ya chikhulupiriro, ndi chikondi chochitachita, ndi chipiriro cha chiyembekezo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu Atate wathu;


Pakuti mukumbukira, abale, chigwiritso chathu ndi chivuto chathu; pochita usiku ndi usana, kuti tingalemetse wina wa inu, tinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu.


Koma, abale, tikupemphani, dziwani iwo akugwiritsa ntchito mwa inu, nakhala akulu anu mwa Ambuye, nakuyambirirani inu;


Akulu akuweruza bwino ayesedwe oyenera ulemu wowirikiza, makamaka iwo akuchititsa m'mau ndi m'chiphunzitso.


Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akachite ndi chimwemwe, osati mwachisoni: pakuti ichi sichikupindulitsani inu.


Perekani moni kwa atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akupatsani moni iwo a ku Italiya.


pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.


Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu. Koma nonsenu muvale kudzichepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo kwa odzichepetsa.


Chifukwa chake ife tiyenera kulandira otere, kuti tikakhale othandizana nacho choonadi.


ndipo uli nacho chipiriro, ndipo walola chifukwa cha dzina langa, wosalema.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa