Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 134 - Buku Lopatulika


Afulumizidwa anthu kulemekeza Yehova
Nyimbo yokwerera.

1 Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse, akuimirira m'nyumba ya Yehova usiku.

2 Kwezani manja anu kumalo oyera, nimulemekeze Yehova.

3 Yehova, ali mu Ziyoni, akudalitseni; ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa