Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 4:28 - Buku Lopatulika

Iyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Geresoni m'chihema chokomanako; ndipo Itamara mwana wa Aroni wansembe ayang'anire udikiro wao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Geresoni m'chihema chokomanako; ndipo Itamara mwana wa Aroni wansembe ayang'anire udikiro wao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Imeneyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Ageresoni m'chihema chamsonkhano, ndipo woyang'anira ntchitoyo akhale Itamara, mwana wa wansembe Aroni.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.

Onani mutuwo



Numeri 4:28
6 Mawu Ofanana  

Ichi ndi chiwerengo cha zinthu za chihema, chihema cha mboni, monga anaziwerenga, monga mwa mau a Mose, achite nazo Alevi; anaziwerenga Itamara, mwana wa Aroni wansembe.


Ntchito yonse ya ana a Ageresoni, kunena za akatundu ao ndi ntchito zao zonse, ikhale monga adzanena Aroni ndi ana ake aamuna; ndipo muwaike adikire akatundu ao onse.


Kunena za ana a Merari, Uwawerenge monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao.


Iyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Merari, monga mwa ntchito zao zonse m'chihema chokomanako, mowauza Itamara mwana wa Aroni wansembe.


Anapatsa ana a Geresoni magaleta awiri ndi ng'ombe zinai, monga mwa ntchito yao;