Numeri 30:12 - Buku Lopatulika
Koma ngati mwamuna wake anazifafanizadi tsiku lakuzimva iye, zonse zotuluka m'milomo yake kunena za zowinda zake, kapena za chodziletsa cha moyo wake sizidzakhazikika; mwamuna wake anafafaniza; ndipo Yehova adzamkhululukira iye.
Onani mutuwo
Koma ngati mwamuna wake anazifafanizadi tsiku lakuzimva iye, zonse zotuluka m'milomo yake kunena za zowinda zake, kapena za chodziletsa cha moyo wake sizidzakhazikika; ndipo Yehova adzamkhululukira iye.
Onani mutuwo
Koma pa tsiku limene mwamuna wake wamva zimenezo, akamletsa mkaziyo kuti asachite zimene adalumbirazo, palibe lamulo lomkakamiza mkaziyo kuchita zimene adalumbira kapenanso zimene adalonjeza. Mwamuna wake waletsa, ndipo Chauta adzamkhululukira mkaziyo.
Onani mutuwo
Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo.
Onani mutuwo