Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 28:5 - Buku Lopatulika

ndi limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosakaniza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndi limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Muziperekanso kilogaramu limodzi la ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta aolivi oyenga bwino okwanira lita limodzi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.

Onani mutuwo



Numeri 28:5
8 Mawu Ofanana  

Koma omeri ndilo limodzi la magawo khumi la efa.


Uperekenso nsembe yaufa pamodzi naye m'mawa ndi m'mawa, limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, ndi limodzi la magawo atatu la hini wa mafuta, kusakaniza ndi ufa wosalala, ndiyo nsembe yaufa ya Yehova kosalekeza, mwa lemba losatha.


Ndipo munthu akabwera nacho chopereka ndicho nsembe yaufa ya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala cha ufa wosalala; ndipo athirepo mafuta, ndi kuikapo lubani.


Mwanawankhosa mmodziyo umpereke m'mawa, ndi mwanawankhosa winayo umpereke madzulo;


Ndiyo nsembe yopsereza kosalekeza, yoikika kuphiri la Sinai, ichite fungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.


chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake ndiko masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwirizo zodzala ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ukhale nsembe yaufa;