Numeri 26:2 - Buku Lopatulika Werenga khamu lonse la ana a Israele, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, monga mwa nyumba za makolo ao, onse akutulukira kunkhondo mu Israele. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Werenga khamu lonse la ana a Israele, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, monga mwa nyumba za makolo ao, onse akutulukira kunkhondo m'Israele. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa “Uchite chiŵerengero cha mpingo wonse wa Aisraele, kuyambira anthu aamuna a zaka makumi aŵiri ndi opitirirapo, potsata mabanja a makolo ao, anthu onse a m'dziko la Israele amene angathe kumenya nkhondo.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.” |