Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 21:27 - Buku Lopatulika

Chifukwa chake iwo akunena mophiphiritsa akuti, Idzani ku Hesiboni, mzinda wa Sihoni umangike, nukhazikike.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chifukwa chake iwo akunena mophiphiritsa akuti, Idzani ku Hesiboni, mudzi wa Sihoni umangike, nukhazikike.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nchifukwa chake oimba ndakatulo amati, “Bwerani ku Hesiboni, mzindawu umangidwenso, tiyeni timange mzinda wa Sihoni kuti ukhazikikenso.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.

Onani mutuwo



Numeri 21:27
6 Mawu Ofanana  

Ndipo atatha kumanga linga, ndinaika zitseko, nakhazika odikira, ndi oimbira, ndi Alevi;


pamenepo udzaimbira mfumu ya ku Babiloni nyimbo iyi yanchinchi, ndi kuti, Wovuta wathadi? Mudzi wagolide wathadi!


Kodi sadzamnenera fanizo onsewo, ndi mwambi womnyodola, ndi kuti, Tsoka iye wochulukitsa zimene sizili zake? Mpaka liti? Iye wodzisenzera zigwiriro.


Chifukwa chake, ananena m'buku la Nkhondo za Yehova, Waheba mu Sufa, ndi miyendo ya Arinoni;


Popeza Hesiboni ndiwo mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, imene idathira nkhondo pa mfumu idafayo ya Mowabu, nilanda dziko lake m'dzanja lake kufikira Arinoni.


Popeza moto unatuluka mu Hesiboni, chirangali cha moto m'mzinda wa Sihoni; chatha Ari wa Mowabu, eni misanje ya Arinoni.