Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 14:42 - Buku Lopatulika

Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Musapite, kuti mungaphedwe pamaso pa adani anu, pakuti Chauta sali nanu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu

Onani mutuwo



Numeri 14:42
9 Mawu Ofanana  

ndipo anatuluka kukomana naye Asa, nanena naye, Mundimvere, Asa, ndi onse Ayuda ndi Abenjamini, Yehova ali nanu; mukakhala ndi Iye, mukamfuna Iye, mudzampeza; koma mukamsiya, adzakusiyani.


Munapinditsa kukamwa kwake kwa lupanga lake, osamuimika kunkhondo.


Pakuti Aamaleke ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, chifukwa chake Yehova sadzakhala nanu.


Koma Yehova anati kwa ine, Nena nao, Musakwerako, kapena kuthira nkhondo; popeza sindili pakati panu; angakukantheni adani anu.


Pamenepo ndidzawapsera mtima tsiku ilo, ndipo ndidzawataya, ndi kuwabisira nkhope yanga, ndipo adzathedwa, ndi zoipa ndi zovuta zambiri zidzawafikira; kotero kuti adzati tsiku lija, Sizitifikira kodi zoipa izi popeza Mulungu wathu sakhala pakati pa ife?


Mwa ichi ana a Israele sangathe kuima pamaso pa adani ao, awafulatira adani ao, pakuti aperekedwa aonongeke. Sindidzakhalanso nanu mukapanda kuononga choperekedwacho, kuchichotsa pakati pa inu.


Ndidzanenanji, Ambuye, Israele atabwerera m'mbuyo pamaso pa adani ao?


Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samisoni. Nagalamuka iye m'tulo take, nati, Ndizituluka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwe kuti Yehova adamchokera.