Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 66:2 - Buku Lopatulika

Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Imbani nyimbo zoyamika dzina lake laulemerero, mumtamande mwaulemu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.

Onani mutuwo



Masalimo 66:2
17 Mawu Ofanana  

Nati Alevi, Yesuwa, ndi Kadimiyele, Bani, Hasabineya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya, ndi Petahiya, Imirirani, lemekezani Yehova Mulungu wanu kunthawi za nthawi; ndipo lilemekezeke dzina lanu la ulemerero, lokuzika loposa chilemekezo ndi chiyamiko chonse.


Adzafotokoza ndani ntchito zamphamvu za Yehova, adzamveketsa ndani chilemekezo chake chonse?


Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake, ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!


Ndipo apereke nsembe zachiyamiko, nafotokozere ntchito zake ndi kufuula mokondwera.


Kwa Iye wakuberekeka pamwambamwamba, oyambira kale lomwe; taonani; amveketsa liu lake, ndilo liu lamphamvu.


Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israele, amene achita zodabwitsa yekhayo.


Tithandizeni Mulungu wa chipulumutso chathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu, chifukwa cha dzina lanu.


Apereke ulemerero kwa Yehova, anene matamando ake m'zisumbu.


Imbani inu, m'mwamba, nukondwere iwe dziko lapansi, imbani inu mapiri, pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ake, nadzachitira chifundo ovutidwa ake.


Ndipo wina anafuula kwa mnzake, nati, Woyera, Woyera, Woyera, Yehova wa makamu; dziko lonse lapansi ladzala ulemerero wake.


Ndipo cholengedwa chilichonse chili m'mwamba, ndi padziko, ndi pansi padziko, ndi m'nyanja, ndi zonse zili momwemo, ndinazimva zilikunena, Kwa Iye wakukhala pa mpando wachifumu, ndi kwa Mwanawankhosa zikhale chiyamiko, ndi ulemu, ndi ulemerero, ndi mphamvu, kufikira nthawi za nthawi.